< Yobu 18 >
1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Y respondió Baldad Sujita, y dijo:
2 “Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
¿Cuándo pondréis fin a las palabras? Entendéd, y después hablemos.
3 Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
¿Por qué somos tenidos por bestias? ¿en vuestros ojos, somos viles?
4 Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
Oh tú que despedazas tu alma con tu furor, ¿será dejada la tierra por tu causa, y serán traspasadas las peñas de su lugar?
5 “Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
Ciertamente la luz de los impíos será apagada, y la centella de su fuego no resplandecerá.
6 Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
La luz se oscurecerá en su tienda, y su candil se apagará sobre él.
7 Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
Los pasos de su potencia serán acortados, y su mismo consejo le echará a perder.
8 Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
Porque red será echada en sus pies, y sobre red andará.
9 Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
Lazo prenderá su calcañar: esforzará contra él a los sedientos.
10 Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
Su cuerda está escondida en la tierra, y su orzuelo sobre la senda.
11 Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
De todas partes le asombrarán temores; y con sus mismos pies le ahuyentarán.
12 Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
Su fuerza será hambrienta, y a su costilla estará aparejado quebrantamiento.
13 Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
Comerá los ramos de su cuero, y el primogénito de la muerte tragará sus miembros.
14 Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
Su confianza será arrancada de su tienda, y le harán llevar al rey de los espantos.
15 Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
En su misma tienda morará como si no fuese suya: piedrazufre será esparcida sobre su morada.
16 Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
Abajo se secarán sus raíces, y arriba serán cortados sus ramos.
17 Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
Su memoria perecerá de la tierra, y no tendrá nombre por las calles.
18 Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
De la luz será lanzado a las tinieblas, y será echado del mundo.
19 Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
No tendrá hijo ni nieto en su pueblo, ni sucesor en sus moradas.
20 Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
Sobre su día se espantarán los por venir, y a los antiguos tomarán pavor.
21 Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”
Ciertamente tales son las moradas del impío, y este es el lugar del que no conoció a Dios.