< Yobu 18 >

1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Respondens autem Baldad Suhites, dixit:
2 “Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
Usque ad quem finem verba jactabitis? intelligite prius, et sic loquamur.
3 Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
Quare reputati sumus ut jumenta, et sorduimus coram vobis?
4 Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
Qui perdis animam tuam in furore tuo, numquid propter te derelinquetur terra, et transferentur rupes de loco suo?
5 “Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
Nonne lux impii extinguetur, nec splendebit flamma ignis ejus?
6 Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
Lux obtenebrescet in tabernaculo illius, et lucerna quæ super eum est extinguetur.
7 Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
Arctabuntur gressus virtutis ejus, et præcipitabit eum consilium suum.
8 Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
Immisit enim in rete pedes suos, et in maculis ejus ambulat.
9 Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
Tenebitur planta illius laqueo, et exardescet contra eum sitis.
10 Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
Abscondita est in terra pedica ejus, et decipula illius super semitam.
11 Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
Undique terrebunt eum formidines, et involvent pedes ejus.
12 Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
Attenuetur fame robur ejus, et inedia invadat costas illius.
13 Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
Devoret pulchritudinem cutis ejus; consumat brachia illius primogenita mors.
14 Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
Avellatur de tabernaculo suo fiducia ejus, et calcet super eum, quasi rex, interitus.
15 Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
Habitent in tabernaculo illius socii ejus qui non est; aspergatur in tabernaculo ejus sulphur.
16 Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
Deorsum radices ejus siccentur: sursum autem atteratur messis ejus.
17 Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
Memoria illius pereat de terra, et non celebretur nomen ejus in plateis.
18 Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
Expellet eum de luce in tenebras, et de orbe transferet eum.
19 Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
Non erit semen ejus, neque progenies in populo suo, nec ullæ reliquiæ in regionibus ejus.
20 Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
In die ejus stupebunt novissimi, et primos invadet horror.
21 Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”
Hæc sunt ergo tabernacula iniqui, et iste locus ejus qui ignorat Deum.

< Yobu 18 >