< Yobu 18 >
1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
シユヒ人ビルダデこたへて曰く
2 “Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
汝等いつまで言語を獵求むることをするや 汝ら先曉るべし 然る後われら辨論はん
3 Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
われら何ぞ獸畜とおもはるべけんや 何ぞ汝らの目に汚穢たる者と見らるべけんや
4 Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
なんぢ怒りて身を裂く者よ 汝のためとて地あに棄られんや 磐あに其處より移されんや
5 “Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
惡き者の光明は滅され 其火の焔は照じ
6 Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
その天幕の内なる光明は暗くなり其が上の燈火は滅さるべし
7 Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
またその強き歩履は狹まり 其計るところは自分を陷いる
8 Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
すなはち其足に逐れて網に到り また陷阱の上を歩むに
9 Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
索はその踵に纒り 羂これを執ふ
10 Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
索かれを執ふるために地に隱しあり 羂かれを陷しいるるために路に設けあり
11 Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
怖ろしき事四方において彼を懼れしめ 其足にしたがひて彼をおふ
12 Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
その力は餓ゑ 其傍には災禍そなはり
13 Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
その膚の肢は蝕壞らる 即ち死の初子これが肢を蝕壞るなり
14 Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
やがて彼はその恃める天幕より曳離されて懼怖の王の許に驅やられん
15 Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
彼に屬せざる者かれの天幕に住み 硫礦かれの家の上に降ん
16 Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
下にてはその根枯れ 上にてはその枝砍る
17 Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
彼の跡は地に絶え 彼の名は街衢に傳はらじ
18 Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
彼は光明の中より黒暗に逐やられ 世の中より驅出されん
19 Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
彼は其民の中に子も無く孫も有じ また彼の住所には一人も遺る者なからん
20 Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
之が日を見るにおいて後に來る者は駭き 先に出し者は怖おそれん
21 Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”
かならず惡き人の住所は是のごとく 神を知ざる者の所は是のごとくなるべし