< Yobu 18 >

1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Et Bildad de Such répondit et dit:
2 “Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
Jusques à quand chasserez-vous aux mots? Prenez du sens, puis nous parlerons!
3 Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
Pourquoi nous tient-on pour des brutes, sommes-nous stupides à vos yeux?
4 Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
Toi, qui dans ta fureur te déchires toi-même, la terre à cause de toi sera-t-elle désertée, et le rocher transporté de sa place?
5 “Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
Aussi bien la lumière des impies s'éteint, et la flamme de son feu cesse de briller;
6 Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
la lumière de sa tente s'éclipse, et sa lampe au-dessus de lui s'éteint;
7 Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
sa vigoureuse allure s'embarrasse, et il se perd par les mesures qu'il prend;
8 Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
car ses pieds mêmes le conduisent au piège, et il marche sur des lacs;
9 Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
le lacet le saisit au talon, et le filet se rend maître de lui;
10 Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
le sol pour lui recouvre des rêts, et la trappe l'attend sur le sentier.
11 Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
De toutes parts des terreurs l'épouvantent, et le pressent par derrière.
12 Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
Le malheur est avide de lui, et la misère s'apprête à le faire tomber.
13 Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
Il dévore les membres de son corps, il dévore ses membres, le Premier-né de la Mort.
14 Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
Il est arraché de sa tente, sa sécurité, et traîné vers le Roi de l'épouvante.
15 Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
D'autres que les siens viennent habiter sa tente, et le soufre tombe en pluie sur sa demeure;
16 Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
à ses pieds ses racines sèchent, à son sommet son rameau se flétrit,
17 Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
sa mémoire disparaît du pays, et il n'a plus un nom dans les campagnes;
18 Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
il est refoulé de la lumière dans la nuit, et banni de la terre;
19 Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
il n'a dans son peuple ni race, ni lignée, et pas un reste de lui dans ses demeures;
20 Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
son jour terrifie la postérité, et fait frissonner les contemporains.
21 Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”
Ainsi seulement finissent les demeures du méchant, et ainsi le séjour de qui méconnaît Dieu.

< Yobu 18 >