< Yobu 18 >

1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Alors Bildad Suhite prit la parole, et dit:
2 “Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
Quand finirez-vous ces discours? écoutez, et puis nous parlerons.
3 Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
Pourquoi sommes-nous regardés comme bêtes, [et] pourquoi nous tenez-vous pour souillés?
4 Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
[Ô toi!] qui te déchires toi-même en ta fureur, la terre sera-t-elle abandonnée à cause de toi, [et] les rochers seront-ils transportés de leur place?
5 “Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
Certainement, la lumière des méchants sera éteinte, et l'étincelle de leur feu ne reluira point.
6 Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
La lumière sera obscurcie dans la tente de chacun d'eux, et la lampe [qui éclairait] au-dessus d'eux sera éteinte.
7 Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
Les démarches de sa force seront resserrées, et son conseil le renversera.
8 Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
Car il sera enlacé par ses pieds dans les filets, et il marchera sur des rets.
9 Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
Le lacet lui saisira le talon, et le voleur le saisissant en aura le dessus.
10 Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
Son piège est caché dans la terre, et sa trappe cachée sur son sentier.
11 Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
Les terreurs l'assiégeront de tous côtés, et le feront trotter çà et là de ses pieds.
12 Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
Sa force sera affamée, et la calamité sera toujours à son côté.
13 Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
Le premier-né de la mort dévorera ce qui soutient sa peau, il dévorera, [dis-je], ce qui le soutient.
14 Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
[Les choses en quoi il mettait] sa confiance seront arrachées de sa tente, et il sera conduit vers le Roi des épouvantements.
15 Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
On habitera dans sa tente, sans qu'elle soit plus à lui; et le soufre sera répandu sur sa maison de plaisance.
16 Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
Ses racines sécheront au dessous, et ses branches seront coupées en haut.
17 Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
Sa mémoire périra sur la terre, et on ne parlera plus de son nom dans les places.
18 Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
On le chassera de la lumière dans les ténèbres, et il sera exterminé du monde.
19 Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
Il n'aura ni fils ni petit-fils parmi son peuple, et il n'aura personne qui lui survive dans ses demeures.
20 Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
Ceux qui seront venus après lui, seront étonnés de son jour; et ceux qui auront été avant lui en seront saisis d'horreur.
21 Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”
Certainement telles seront les demeures du pervers, et tel sera le lieu de celui qui n'a point reconnu le [Dieu] Fort.

< Yobu 18 >