< Yobu 18 >

1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Then Baldad the Suhite answered, and said:
2 “Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
How long will you throw out words? understand first, and so let us speak.
3 Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
Why are we reputed as beasts, and counted vile before you?
4 Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
Thou that destroyest thy soul in thy fury, shall the earth be forsaken for thee, and shall rocks be removed out of their place?
5 “Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
Shall not the light of the wicked be extinguished, and the flame of his fire not shine?
6 Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
The light shall be dark in his tabernacle, and the lamp that is over him, shall be put out.
7 Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
The step of his strength shall be straitened, and his own counsel shall cast him down headlong.
8 Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
For he hath thrust his feet into a net, and walketh in its meshes.
9 Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
The sole of his foot shall be held in a snare, and thirst shall burn against him.
10 Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
A gin is hidden for him in the earth, and his trap upon the path.
11 Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
Fears shall terrify him on every side, and shall entangle his feet.
12 Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
Let his strength be wasted with famine, and let hunger invade his ribs.
13 Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
Let it devour the beauty of his skin, let the firstborn death consume his arms.
14 Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
Let his confidence be rooted out of his tabernacle, and let destruction tread upon him like a king.
15 Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
Let the companions of him that is not, dwell in his tabernacle, let brimstone be sprinkled in his tent.
16 Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
Let his roots be dried up beneath, and his harvest destroyed above.
17 Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
Let the memory of him perish from the earth and let not his name be renowned in the streets.
18 Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
He shall drive him out of light into darkness, and shall remove him out of the world.
19 Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
His seed shall not subsist, nor his offspring among his people, nor any remnants in his country.
20 Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
They that come after him shall be astonished at his day, and horror shall fall upon them that went before.
21 Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”
These men are the tabernacles of the wicked, and this the place of him that knoweth not God.

< Yobu 18 >