< Yobu 18 >
1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
But Baldad the Suhite responded by saying:
2 “Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
How long will you throw around words? Understand first, and then let us speak.
3 Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
Why have we been treated like mules, as if we were unworthy before you?
4 Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
You, who ruins your own soul in your fury, will the earth be forsaken because of you, and will the cliffs be moved from their place?
5 “Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
Will not the light of the impious be put out, and the flame of his fire refuse to shine?
6 Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
Light will become darkness in his tabernacle, and the lamp that is over him will be extinguished.
7 Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
His strong steps will be constrained, and his own counsel will cast him down uncontrollably.
8 Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
For he has caused his own feet to go into a net, and he has walked into its web.
9 Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
His heel will be held in a snare, and thirst will rage against him.
10 Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
A trap has been hidden for him in the earth, and a decoy, along his path.
11 Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
Horrifying things will terrify him everywhere and will entangle his feet.
12 Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
Let his strength be diminished by famine, and let starvation invade his ribs.
13 Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
Let it devour the beauty of his skin; let the ancient death consume his arms.
14 Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
Let his confidence be torn away from his tabernacle, and let ruin trample over him like a king.
15 Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
Let the companions of he who is not, dwell in his tabernacle; let brimstone rain down upon his tabernacle.
16 Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
Let his roots be dried up from beneath him, and his harvest be crushed from above.
17 Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
Let the memory of him perish from the earth, and let not his name be celebrated in the streets.
18 Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
He will expel him from light into darkness, and he will remove him from the world.
19 Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
Neither his offspring, nor his descendants, will exist among his people, nor will there be any remnants in his country.
20 Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
The last will be astonished at his day, and the first will be overcome with horror.
21 Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”
And so, these are the tabernacles of the sinful, and this the place of he who does not know God.