< Yobu 18 >
1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Saa tog Sjuhiten Bildad til Orde og sagde:
2 “Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
Saa gør dog en Ende paa dine Ord, kom til Fornuft og lad os tale!
3 Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
Hvi skal vi regnes for Kvæg og staa som umælende i dine Øjne?
4 Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
Du, som i Vrede sønderslider din Sjæl, skal for din Skyld Jorden blive øde og Klippen flyttes fra sit Sted?
5 “Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
Nej, den gudløses Lys bliver slukt, hans Ildslue giver ej Lys;
6 Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
Lyset i hans Telt gaar ud, og hans Lampe slukkes for ham;
7 Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
hans kraftige Skridt bliver korte, han falder for eget Raad;
8 Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
thi hans Fod drives ind i Nettet, paa Fletværk vandrer han frem,
9 Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
Fælden griber om Hælen, Garnet holder ham fast;
10 Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
Snaren er skjult i Jorden for ham og Saksen paa hans Sti;
11 Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
Rædsler skræmmer ham alle Vegne og kyser ham Skridt for Skridt:
12 Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
Ulykken hungrer efter ham, Undergang lurer paa hans Fald:
13 Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
Dødens førstefødte æder hans Lemmer, æder hans Legemes Lemmer;
14 Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
han rives bort fra sit Telt, sin Fortrøstning; den styrer hans Skridt til Rædslernes Konge;
15 Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
i hans Telt har Undergang hjemme, Svovl strøs ud paa hans Bolig;
16 Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
nedentil tørrer hans Rødder, oventil visner hans Grene;
17 Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
hans Minde svinder fra Jord, paa Gaden nævnes ikke hans Navn;
18 Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
man støder ham ud fra Lys i Mørket og driver ham bort fra Jorderig;
19 Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
i sit Folk har han ikke Afkom og Æt, i hans Hjem er der ingen tilbage;
20 Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
de i Vester stivner ved hans Skæbnedag, de i Øst bliver slagne af Rædsel.
21 Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”
Ja, saaledes gaar det den lovløses Bolig, dens Hjem, der ej kender Gud!