< Yobu 18 >

1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha kuti,
Odpovídaje pak Bildad Suchský, řekl:
2 “Kodi iwe Yobu utsiriza liti zoyankhula zakozi? Khala munthu wozindikira zinthu ndipo ukatero ife tidzayankhula.
Dokudž neučiníte konce řečem? Pomyslte na to, a potom mluviti budeme.
3 Chifukwa chiyani ukutiyesa ngati ngʼombe ndi kuoneka ngati opusa mʼmaso mwako?
Proč jsme počteni za hovada? Oškliví jsme jemu, jakž sami vidíte.
4 Iwe amene ukudzipweteka wekha ndi mkwiyo wako, kodi dziko lapansi lisanduke bwinja chifukwa cha iweyo? Kodi kapena thanthwe lisunthidwe kuchoka pa malo ake?
Ó ty, jenž hubíš život svůj zůřením svým, zdaliž pro tebe opuštěna bude země, a odsedne skála z místa svého?
5 “Nyale ya munthu woyipa yazimitsidwa; malawi a moto wake sakuwalanso.
Anobrž světlo bezbožných uhašeno bude, aniž se blyštěti bude jiskra ohně jejich.
6 Kuwala kwa mʼnyumba mwake kwasanduka mdima; nyale ya pambali pake yazima.
Světlo se zatmí v stánku jeho, a lucerna jeho v něm zhasne.
7 Mayendedwe ake amgugu azilala; fundo zake zomwe zamugwetsa.
Ssouženi budou krokové síly jeho, a porazí jej rada jeho.
8 Mapazi ake amulowetsa mu ukonde ndipo akungoyendayenda mu ukondewo.
Nebo zapleten jest do síti nohami svými, a v zamotání chodí.
9 Msampha wamkola mwendo; khwekhwe lamugwiritsitsa.
Chytí ho za patu osídlo, a zmocní se ho násilník.
10 Amutchera msampha pansi mobisika; atchera diwa pa njira yake.
Skrytať jest při zemi smečka jeho, a léčka jeho na stezce.
11 Zoopsa zikumuchititsa mantha kumbali zonse, zikutsatira mayendedwe ake onse.
Odevšad hrůzy jej děsiti budou a dotírati na nohy jeho.
12 Mphamvu zake zatha chifukwa cha njala, tsoka likumudikira.
Hladovitá bude síla jeho, a bída pohotově při boku jeho.
13 Wagwidwa nthenda yoopsa thupi lonse; miyendo yake, manja ake, zonse zawola.
Zžíře žily kůže jeho, zžíře oudy jeho kníže smrti.
14 Wachotsedwa mʼnyumba imene ankadalira, ndipo amukokera ku imfa, mfumu ya zoopsa zonse.
Uchváceno bude z stánku jeho doufání jeho, a to jej přivede k králi strachů.
15 Mʼnyumba mwake zonse zachotsedwamo; awazamo sulufule kuti aphe tizirombo ta matenda.
V stánku jeho hrůza bydleti bude, ač nebyl jeho; posypáno bude obydlí jeho sirou.
16 Mizu yake ikuwuma pansi ndipo nthambi zake zikufota
Od zpodku kořenové jeho uschnou, a svrchu osekány budou ratolesti jeho.
17 Sadzakumbukiridwanso pa dziko lapansi; sadzakhalanso ndi chinthu chomutchukitsa mʼdziko.
Památka jeho zahyne z země, aniž jméno jeho slýcháno bude na ulicích.
18 Amuchotsa pa malo owala ndi kumuponya ku mdima, ndipo amupirikitsa pa dziko lonse.
Vyženou ho z světla do tmy, anobrž z okršlku zemského vypudí jej.
19 Iye alibe ana kapena zidzukulu pakati pa anthu ake, kulibe wotsala kumene iye ankakhala.
Nepozůstaví ani syna ani vnuka v lidu svém, ani jakého ostatku v příbytcích svých.
20 Anthu akumadzulo adabwa kwambiri ndi tsoka lake; anthu akummawa agwidwa ndi mantha aakulu.
Nade dnem jeho zděsí se potomci, a přítomní strachem podjati budou.
21 Ndithudi, izi ndiye zimagwera munthu woyipa; amenewa ndiye mathero a munthu amene sadziwa Mulungu.”
Takovýť jest zajisté způsob nešlechetného, a takový cíl toho, kterýž nezná Boha silného.

< Yobu 18 >