< Yobu 17 >
1 “Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
Mi alma se agota, mis días se extinguen. El sepulcro está preparado para mí.
2 Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
No hay conmigo sino burladores, y mis ojos se fijan en su provocación.
3 “Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
Te ruego, deposita una fianza ante Ti mismo. ¿Quién quiere ser mi garante?
4 Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
Porque cerraste su corazón al entendimiento. Por tanto, no los exaltarás.
5 Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
Al que traiciona a sus amigos por recompensa, les desfallecerán los ojos a sus hijos.
6 “Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
Pero Él me convirtió en un refrán de la gente. Soy uno a quien los hombres escupen.
7 Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
Mis ojos se oscurecieron por la angustia, y todos mis miembros son como una sombra.
8 Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
Los rectos se asombran de esto, y el inocente se levanta contra el impío.
9 Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
Sin embargo, el justo se aferra a su camino, y el limpio de manos aumentará sus fuerzas.
10 “Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
Pero ahora, vuelvan todos ustedes y vengan acá. Pero entre ustedes no hallaré algún sabio.
11 Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
Mis días pasaron. Mis planes se deshicieron, aun los anhelos de mi corazón
12 Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
que solían cambiar la noche en día. La luz está después de la oscuridad.
13 Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol )
Si espero, yo sé que el Seol es mi habitación. En la tenebrosidad tengo extendida mi cama. (Sheol )
14 ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
A la descomposición digo: ¡Padre mío! Y al gusano: ¡Madre mía, hermana mía!
15 tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
¿Dónde está entonces mi esperanza? ¿Quién verá mi bien?
16 Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol )
Descenderá conmigo al Seol y juntos bajaremos al polvo. (Sheol )