< Yobu 17 >

1 “Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
Min ånd er brutt, mine dager utslukket; bare graver har jeg for mig.
2 Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
Sannelig, spott omgir mig på alle kanter, og mitt øie må dvele ved deres trettekjære ferd.
3 “Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
Så sett nu et pant, gå i borgen for mig hos dig selv! Hvem skulde ellers gi mig håndslag?
4 Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
Du har jo lukket deres hjerte for innsikt; derfor vil du ikke la dem vinne.
5 Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
Den som forråder venner, så de blir til bytte, hans barns øine skal tæres bort.
6 “Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
Jeg er satt til et ordsprog for folk; jeg er en mann som blir spyttet i ansiktet.
7 Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
Mitt øie er sløvt av gremmelse, og alle mine lemmer er som en skygge.
8 Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
Rettskafne forferdes over dette, og den skyldfrie harmes over den gudløse;
9 Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
men den rettferdige holder fast ved sin vei, og den som har rene hender, får enn mere kraft.
10 “Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
Men I - kom bare igjen alle sammen! Jeg finner dog ikke nogen vismann blandt eder.
11 Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
Mine dager er faret forbi, mine planer sønderrevet - mitt hjertes eiendom!
12 Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
Natt gjør de til dag, lyset, sier de, er nærmere enn det mørke som ligger like for mig.
13 Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol h7585)
Når jeg håper på dødsriket som mitt hus, reder i mørket mitt leie, (Sheol h7585)
14 ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
roper til graven: Du er min far, til makken: Du er min mor og min søster,
15 tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
hvor er da mitt håp? Mitt håp - hvem øiner det?
16 Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol h7585)
Til dødsrikets bommer farer de ned, på samme tid som jeg går til hvile i støvet. (Sheol h7585)

< Yobu 17 >