< Yobu 17 >

1 “Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
Mein Odem ist schwach, und meine Tage sind abgekürzt; das Grab ist da.
2 Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
Fürwahr, Gespött umgibt mich, und auf ihrem Hadern muß mein Auge weilen.
3 “Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
Sei du selber mein Bürge bei dir; wer will mich sonst vertreten?
4 Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
Denn du hast ihrem Herzen den Verstand verborgen; darum wirst du ihnen den Sieg geben.
5 Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
Es rühmt wohl einer seinen Freunden die Ausbeute; aber seiner Kinder Augen werden verschmachten.
6 “Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
Er hat mich zum Sprichwort unter den Leuten gemacht, und ich muß mir ins Angesicht speien lassen.
7 Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
Mein Auge ist dunkel geworden vor Trauern, und alle meine Glieder sind wie ein Schatten.
8 Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
Darüber werden die Gerechten sich entsetzen, und die Unschuldigen werden sich entrüsten gegen die Heuchler.
9 Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
Aber der Gerechte wird seinen Weg behalten; und wer reine Hände hat, wird an Stärke zunehmen.
10 “Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
Wohlan, so kehrt euch alle her und kommt; ich werde doch keinen Weisen unter euch finden.
11 Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
Meine Tage sind vergangen; meine Anschläge sind zerrissen, die mein Herz besessen haben.
12 Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
Sie wollen aus der Nacht Tag machen und aus dem Tage Nacht.
13 Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol h7585)
Wenn ich gleich lange harre, so ist doch bei den Toten mein Haus, und in der Finsternis ist mein Bett gemacht; (Sheol h7585)
14 ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
Die Verwesung heiße ich meinen Vater und die Würmer meine Mutter und meine Schwester:
15 tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
was soll ich denn harren? und wer achtet mein Hoffen?
16 Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol h7585)
Hinunter zu den Toten wird es fahren und wird mit mir in dem Staub liegen. (Sheol h7585)

< Yobu 17 >