< Yobu 17 >

1 “Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
My breath is corrupt, my days are extinct, the graves [are ready] for me.
2 Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
[Are there] not mockers with me? and doth not my eye continue in their provocation?
3 “Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
Lay down now, put me in a surety with thee; who [is] he [that] will strike hands with me?
4 Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
For thou hast hid their heart from understanding: therefore shalt thou not exalt [them].
5 Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
He that speaketh flattery to [his] friends, even the eyes of his children shall fail.
6 “Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
He hath made me also a by-word of the people; and in former time I was as a tabret.
7 Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
My eye also is dim by reason of sorrow, and all my members [are] as a shade.
8 Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
Upright [men] shall be astonished at this, and the innocent shall stir up himself against the hypocrite.
9 Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
The righteous also shall hold on his way, and he that hath clean hands shall be stronger and stronger.
10 “Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
But as for you all, do ye return, and come now: for I cannot find [one] wise [man] among you.
11 Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
My days are past, my purposes are broken off, [even] the thoughts of my heart.
12 Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
They change the night into day: the light [is] short because of darkness.
13 Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol h7585)
If I wait, the grave [is] my house: I have made my bed in the darkness. (Sheol h7585)
14 ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
I have said to corruption, Thou [art] my father: to the worm, [Thou art] my mother, and my sister.
15 tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
And where [is] now my hope? as for my hope, who will see it?
16 Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol h7585)
They shall go down to the bars of the pit, when [our] rest together [is] in the dust. (Sheol h7585)

< Yobu 17 >