< Yobu 17 >
1 “Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
spirit my to destroy day my to extinguish grave to/for me
2 Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
if: surely yes not mockery with me me and in/on/with to rebel they to lodge eye my
3 “Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
to set: put [emph?] please to pledge me with you who? he/she/it to/for hand: themselves my to blow
4 Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
for heart their to treasure from understanding upon so not to exalt
5 Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
to/for portion to tell neighbor and eye son: child his to end: expend
6 “Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
and to set me to/for byword people and spit to/for face: before to be
7 Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
and to grow dim from vexation eye my and member my like/as shadow all their
8 Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
be desolate: appalled upright upon this and innocent upon profane to rouse
9 Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
and to grasp righteous way: conduct his and pure hand to add strength
10 “Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
and but all their to return: return and to come (in): come please and not to find in/on/with you wise
11 Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
day my to pass wickedness my to tear possession heart my
12 Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
night to/for day to set: make light near from face: before darkness
13 Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol )
if to await hell: Sheol house: home my in/on/with darkness to spread bed my (Sheol )
14 ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
to/for pit: grave to call: call out father my you(m. s.) mother my and sister my to/for worm
15 tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
and where? then hope my and hope my who? to see her
16 Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol )
alone: pole hell: Sheol to go down if: surely no unitedness upon dust to descend (Sheol )