< Yobu 17 >
1 “Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
My spirit is consumed, my days are extinct, the grave is [ready] for me.
2 Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
Surely there are mockers with me, and mine eye abideth in their provocation.
3 “Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
Give now a pledge, be surety for me with thyself; who is there that will strike hands with me?
4 Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
For thou hast hid their heart from understanding: therefore shalt thou not exalt [them].
5 Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
He that denounceth his friends for a prey, even the eyes of his children shall fail.
6 “Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
He hath made me also a byword of the people; and I am become an open abhorring.
7 Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
Mine eye also is dim by reason of sorrow, and all my members are as a shadow.
8 Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
Upright men shall be astonied at this, and the innocent shall stir up himself against the godless.
9 Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
Yet shall the righteous hold on his way, and he that hath clean hands shall wax stronger and stronger.
10 “Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
But return ye, all of you, and come now: and I shall not find a wise man among you.
11 Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
My days are past, my purposes are broken off, even the droughts of my heart.
12 Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
They change the night into a day: the fight, [say they], is near unto the darkness.
13 Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol )
If I look for Sheol as mine house; if I have spread my couch in the darkness; (Sheol )
14 ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
If I have said to corruption, Thou art my father; to the worm, [Thou art] my mother, and my sister;
15 tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
Where then is my hope? and as for my hope, who shall see it?
16 Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol )
It shall go down to the bars of Sheol, when once there is rest in the dust. (Sheol )