< Yobu 17 >

1 “Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
Mijn geest gebroken, mijn dagen geblust, Mij rest slechts het graf!
2 Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
Ben ik niet het mikpunt van spot, Verkwijnt niet mijn oog door de bittere verwijten?
3 “Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
Stel Uzelf bij U tot borg voor mijl; Wie anders zou voor mij handslag geven?
4 Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
Want hùn hart hebt Gij voor inzicht gesloten, En daarom steken zij de hand niet uit;
5 Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
Men beklaagt het lot van zijn vrienden Terwijl de ogen versmachten van de eigen kinderen;
6 “Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
Men heeft mij tot spreekwoord gemaakt bij de mensen, Ik ben een, wien men in het aangezicht spuwt!
7 Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
Mijn oog is dof van verdriet, Mijn leden zijn tot een schaduw vervluchtigd!
8 Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
De braven ontstellen ervan, De onschuldige is jaloers op den boze:
9 Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
Moet de rechtvaardige toch zijn weg maar bewandelen, Wie rein van handen is, zijn kracht nog verdubbelen?
10 “Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
En daarom, hoe gij u allen wendt of keert, Een wijze vind ik onder u niet;
11 Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
Mijn levensdagen zijn voorbij, Mijn plannen, mijn hartewensen vernield!
12 Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
Men maakt een dag van de nacht, Van duisternis het morgenlicht!
13 Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol h7585)
Kan ik nog hopen? Het dodenrijk is mijn huis, In de duisternis heb ik mijn leger gespreid; (Sheol h7585)
14 ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
Tot het graf geroepen: Gij zijt mijn vader, Tot de wormen: Gij zijt mijn moeder en zusters!
15 tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
Waar is mijn hoop, Mijn geluk, wie kan het ontdekken:
16 Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol h7585)
Zullen ze met mij in het dodenrijk dalen, Zinken wij samen neer in het stof? (Sheol h7585)

< Yobu 17 >