< Yobu 17 >
1 “Mtima wanga wasweka, masiku anga atha, manda akundidikira.
我的心灵消耗,我的日子灭尽; 坟墓为我预备好了。
2 Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira; maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.
真有戏笑我的在我这里, 我眼常见他们惹动我。
3 “Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna. Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
愿主拿凭据给我,自己为我作保。 在你以外谁肯与我击掌呢?
4 Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu; choncho simudzawalola kuti apambane.
因你使他们心不明理, 所以你必不高举他们。
5 Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma, ana ake sadzaona mwayi.
控告他的朋友、以朋友为可抢夺的, 连他儿女的眼睛也要失明。
6 “Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense, munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
神使我作了民中的笑谈; 他们也吐唾沫在我脸上。
7 Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni; ndawonda ndi mutu womwe.
我的眼睛因忧愁昏花; 我的百体好像影儿。
8 Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi; anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
正直人因此必惊奇; 无辜的人要兴起攻击不敬虔之辈。
9 Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo, ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.
然而,义人要持守所行的道; 手洁的人要力上加力。
10 “Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo, sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
至于你们众人,可以再来辩论吧! 你们中间,我找不着一个智慧人。
11 Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka, pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
我的日子已经过了; 我的谋算、我心所想望的已经断绝。
12 Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana, nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
他们以黑夜为白昼, 说:亮光近乎黑暗。
13 Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda, ngati ndiyala bedi langa mu mdima, (Sheol )
我若盼望阴间为我的房屋, 若下榻在黑暗中, (Sheol )
14 ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’ ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
若对朽坏说:你是我的父; 对虫说:你是我的母亲姊妹;
15 tsono chiyembekezo changa chili kuti? Ndani angaone populumukira panga?
这样,我的指望在哪里呢? 我所指望的谁能看见呢?
16 Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse, polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.” (Sheol )
等到安息在尘土中, 这指望必下到阴间的门闩那里了。 (Sheol )