< Yobu 16 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Y Job respondió y dijo:
2 “Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
Con frecuencia me llegan a los oídos tales cosas; son consoladores que solo dan problemas.
3 Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
¿Pueden las palabras que son como el viento ser detenidas? ¿O qué te anima a darles respuesta?
4 Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
No sería difícil para mí decir tales cosas si sus almas estuvieran en el lugar de mi alma; recopilando palabras contra ustedes y movería sobre ustedes mi cabeza.
5 Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
Podría darte ánimo con mi boca, y el consejo de mis labios apaciguar tu dolor.
6 “Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
Si digo lo que tengo en mente, mi dolor no se reduce: y si me callo, ¿cuánto de eso va a salir de mí?
7 Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
Pero ahora él me ha vencido con cansancio y temor, y tu has asolado toda mi compañía.
8 Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
Me has arrugado, ha surgido como testigo contra mí la flacura, se levanta como testigo a mi rostro.
9 Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
Estoy quebrantado por su ira, y su odio me persigue, ha afilado sus dientes contra mí; mis enemigos me miran con ojos crueles;
10 Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
Sus bocas se mofan contra mí, los golpes de sus palabras amargas están cayendo en mi cara; burlones, todos ellos se juntan a una contra mí.
11 Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
Dios me entrega al poder de los pecadores, enviándome violentamente a las manos de los malhechores.
12 Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
Estaba tranquilo, pero sus manos me habían quebrantado; me ha cogido por el cuello, sacudiéndome en pedazos; Él me ha puesto como una marca para sus flechas.
13 anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
Sus arqueros me rodean; Sus flechas atraviesan mis riñones sin piedad, mi hiel se esparce en la tierra.
14 Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
Estoy quebrado de herida tras herida; viene corriendo hacia mí como un hombre de guerra.
15 “Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
He cosido cilicio sobre mi piel, y mi fuerza está hundida en el polvo.
16 Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
Mi cara está roja de llanto, y en mis ojos está la sombra de muerte;
17 komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
Aunque mis manos no han hecho actos violentos, y mi oración es limpia.
18 “Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
¡Oh tierra, que no se cubra mi sangre, y que mi clamor no tenga lugar de descanso!
19 Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
Aun ahora mi testigo está en el cielo, y mi testimonio está en lo alto.
20 Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
Mis amigos se burlan de mi, a Dios están llorando mis ojos,
21 iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
Oh! que alguien intercediera por un hombre con Dios, como un hombre lo hace por su prójimo.
22 “Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”
Porque los años contados vendrán, en poco tiempo me iré al viaje del cual no volveré.