< Yobu 16 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Entonces Job respondió:
2 “Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
Oí muchas cosas como éstas. Consoladores molestos son todos ustedes.
3 Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
¿Habrá fin para las palabras vanas? ¿Qué te incita a responder?
4 Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
Yo también podría hablar como ustedes. Si su alma estuviera en lugar de la mía, podría hilvanar vocablos contra ustedes y menear la cabeza contra ustedes.
5 Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
Pero los alentaría con mis palabras, y la consolación de mis labios calmaría su dolor.
6 “Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
Si hablo, no cesa mi dolor. Si me abstengo, ¿se aleja de mí?
7 Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
Ahora me agotó. Desoló a toda mi compañía.
8 Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
Colocaste una mano firme contra mí y me llenaste de arrugas, lo cual es un testigo contra mí. Mi flacura es una evidencia adicional que testifica en mi cara.
9 Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
Mi adversario lanzó su mirada contra mí. Me odió, me persiguió, su furor me destrozó, contra mí cruje sus dientes, fija sus ojos contra mí,
10 Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
abren sus bocas contra mí, hieren mis mejillas con afrenta, se unieron contra mí.
11 Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
ʼElohim me entregó a los perversos y me empujó hacia las manos de los impíos.
12 Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
Yo estaba tranquilo, pero Él me quebrantó. Me agarró por el cuello, me destrozó y me colocó como blanco de sus flechas.
13 anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
Sus arqueros me rodearon, atraviesan mis riñones y no perdonan. Derraman mi hiel a tierra,
14 Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
abren brecha tras brecha en mí y arremeten contra mí como un guerrero.
15 “Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
Cosí tela áspera sobre mi piel y coloqué mi cabeza en el polvo.
16 Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
Mi cara está enrojecida de tanto llorar. Sobre mis párpados se afirma la sombra de la muerte,
17 komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
aunque no hubo violencia en mis manos, y fue pura mi oración.
18 “Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
¡Oh tierra, no encubras mi sangre, ni haya lugar de reposo para mi clamor!
19 Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
Ciertamente ahora mi testigo está en el cielo, en las alturas, el que atestigua a mi favor.
20 Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
Mis amigos son mis burladores. Mis ojos lloran ante ʼElohim.
21 iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
¡Ojalá pudiera disputar el hombre ante ʼElohim, como un hombre con su prójimo!
22 “Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”
Porque cuando pasen algunos años, me iré por el camino que no tiene regreso.

< Yobu 16 >