< Yobu 16 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
پس ایوب در جواب گفت:۱
2 “Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
«بسیارچیزها مثل این شنیدم. تسلی دهندگان مزاحم همه شما هستید.۲
3 Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
آیا سخنان باطل راانتها نخواهد شد؟ و کیست که تو را به جواب دادن تحریک می‌کند؟۳
4 Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
من نیز مثل شمامی توانستم بگویم، اگر جان شما در جای جان من می‌بود، و سخنها به ضد شما ترتیب دهم، و سرخود را بر شما بجنبانم،۴
5 Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
لیکن شما را به دهان خود تقویت می‌دادم و تسلی لبهایم غم شما رارفع می‌نمود.۵
6 “Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
«اگر من سخن گویم، غم من رفع نمی گردد؛ واگر ساکت شوم مرا چه راحت حاصل می‌شود؟۶
7 Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
لیکن الان او مرا خسته نموده است. تو تمامی جماعت مرا ویران ساخته‌ای.۷
8 Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
مرا سخت گرفتی و این بر من شاهد شده است. و لاغری من به ضدمن برخاسته، روبرویم شهادت می‌دهد.۸
9 Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
در غضب خود مرا دریده و بر من جفا نموده است. دندانهایش را بر من افشرده و مثل دشمنم چشمان خود را بر من تیز کرده است.۹
10 Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
دهان خود را بر من گشوده‌اند، بر رخسار من به استحقارزده‌اند، به ضد من با هم اجتماع نموده‌اند.۱۰
11 Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
خدامرا به‌دست ظالمان تسلیم نموده، و مرا به‌دست شریران افکنده است.۱۱
12 Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
چون در راحت بودم مراپاره پاره کرده است، و گردن مرا گرفته، مرا خردکرده، و مرا برای هدف خود نصب نموده است.۱۲
13 anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
تیرهایش مرا احاطه کرد. گرده هایم را پاره می‌کند و شفقت نمی نماید. و زهره مرا به زمین می‌ریزد.۱۳
14 Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
مرا زخم بر زخم، مجروح می‌سازد ومثل جبار، بر من حمله می‌آورد.۱۴
15 “Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
بر پوست خود پلاس دوخته‌ام، و شاخ خود را در خاک خوار نموده‌ام.۱۵
16 Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
روی من از گریستن سرخ شده است، و بر مژگانم سایه موت است.۱۶
17 komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
اگر‌چه هیچ بی‌انصافی در دست من نیست، و دعای من پاک است.۱۷
18 “Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
‌ای زمین خون مرا مپوشان، واستغاثه مرا آرام نباشد.۱۸
19 Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
اینک الان نیز شاهد من در آسمان است، و گواه من در اعلی علیین.۱۹
20 Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
دوستانم مرا استهزا می‌کنند، لیکن چشمانم نزد خدا اشک می‌ریزد.۲۰
21 iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
و آیا برای انسان نزدخدا محاجه می‌کند، مثل بنی آدم که برای همسایه خود می‌نماید؟۲۱
22 “Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”
زیرا سالهای اندک سپری می‌شود، پس به راهی که برنمی گردم، خواهم رفت.۲۲

< Yobu 16 >