< Yobu 16 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Respondens autem Job, dixit:
2 “Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
Audivi frequenter talia: consolatores onerosi omnes vos estis.
3 Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
Numquid habebunt finem verba ventosa? aut aliquid tibi molestum est, si loquaris?
4 Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
Poteram et ego similia vestri loqui, atque utinam esset anima vestra pro anima mea: consolarer et ego vos sermonibus, et moverem caput meum super vos;
5 Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
roborarem vos ore meo, et moverem labia mea, quasi parcens vobis.
6 “Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
Sed quid agam? Si locutus fuero, non quiescet dolor meus, et si tacuero, non recedet a me.
7 Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
Nunc autem oppressit me dolor meus, et in nihilum redacti sunt omnes artus mei.
8 Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
Rugæ meæ testimonium dicunt contra me, et suscitatur falsiloquus adversus faciem meam, contradicens mihi.
9 Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
Collegit furorem suum in me, et comminans mihi, infremuit contra me dentibus suis: hostis meus terribilibus oculis me intuitus est.
10 Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
Aperuerunt super me ora sua, et exprobrantes percusserunt maxillam meam: satiati sunt pœnis meis.
11 Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
Conclusit me Deus apud iniquum, et manibus impiorum me tradidit.
12 Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
Ego ille quondam opulentus, repente contritus sum: tenuit cervicem meam, confregit me, et posuit me sibi quasi in signum.
13 anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
Circumdedit me lanceis suis; convulneravit lumbos meos: non pepercit, et effudit in terra viscera mea.
14 Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
Concidit me vulnere super vulnus: irruit in me quasi gigas.
15 “Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
Saccum consui super cutem meam, et operui cinere carnem meam.
16 Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
Facies mea intumuit a fletu, et palpebræ meæ caligaverunt.
17 komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
Hæc passus sum absque iniquitate manus meæ, cum haberem mundas ad Deum preces.
18 “Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
Terra, ne operias sanguinem meum, neque inveniat in te locum latendi clamor meus:
19 Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
ecce enim in cælo testis meus, et conscius meus in excelsis.
20 Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
Verbosi amici mei: ad Deum stillat oculus meus:
21 iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
atque utinam sic judicaretur vir cum Deo, quomodo judicatur filius hominis cum collega suo.
22 “Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”
Ecce enim breves anni transeunt, et semitam per quam non revertar ambulo.