< Yobu 16 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Then Job answered,
2 “Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
“I have heard many such things. You are all miserable comforters!
3 Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
Shall vain words have an end? Or what provokes you that you answer?
4 Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
I also could speak as you do. If your soul were in my soul’s place, I could join words together against you, and shake my head at you,
5 Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
but I would strengthen you with my mouth. The solace of my lips would relieve you.
6 “Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
“Though I speak, my grief is not subsided. Though I forbear, what am I eased?
7 Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
But now, God, you have surely worn me out. You have made all my company desolate.
8 Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
You have shriveled me up. This is a witness against me. My leanness rises up against me. It testifies to my face.
9 Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
He has torn me in his wrath and persecuted me. He has gnashed on me with his teeth. My adversary sharpens his eyes on me.
10 Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
They have gaped on me with their mouth. They have struck me on the cheek reproachfully. They gather themselves together against me.
11 Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
God delivers me to the ungodly, and casts me into the hands of the wicked.
12 Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
I was at ease, and he broke me apart. Yes, he has taken me by the neck, and dashed me to pieces. He has also set me up for his target.
13 anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
His archers surround me. He splits my kidneys apart, and does not spare. He pours out my bile on the ground.
14 Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
He breaks me with breach on breach. He runs at me like a giant.
15 “Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
I have sewed sackcloth on my skin, and have thrust my horn in the dust.
16 Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
My face is red with weeping. Deep darkness is on my eyelids,
17 komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
although there is no violence in my hands, and my prayer is pure.
18 “Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
“Earth, don’t cover my blood. Let my cry have no place to rest.
19 Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
Even now, behold, my witness is in heaven. He who vouches for me is on high.
20 Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
My friends scoff at me. My eyes pour out tears to God,
21 iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
that he would maintain the right of a man with God, of a son of man with his neighbor!
22 “Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”
For when a few years have come, I will go the way of no return.

< Yobu 16 >