< Yobu 16 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Then Job answered and said:
2 “Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
I have heard many such things; sorry comforters are ye all.
3 Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
Shall windy words have an end? Or what provoketh thee that thou answerest?
4 Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
I also could speak as ye do; if your soul were in my soul's stead, I could join words together against you, and shake my head at you.
5 Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
I would strengthen you with my mouth, and the moving of my lips would assuage your grief.
6 “Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
Though I speak, my pain is not assuaged; and though I forbear, what am I eased?
7 Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
But now He hath made me weary; Thou hast made desolate all my company.
8 Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
And Thou hast shrivelled me up, which is a witness against me; and my leanness riseth up against me, it testifieth to my face.
9 Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
He hath torn me in His wrath, and hated me; He hath gnashed upon me with His teeth; mine adversary sharpeneth his eyes upon me.
10 Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
They have gaped upon me with their mouth; they have smitten me upon the cheek scornfully; they gather themselves together against me.
11 Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
God delivereth me to the ungodly, and casteth me into the hands of the wicked.
12 Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
I was at ease, and He broke me asunder; yea, He hath taken me by the neck, and dashed me to pieces; He hath also set me up for His mark.
13 anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
His archers compass me round about, He cleaveth my reins asunder, and doth not spare; He poureth out my gall upon the ground.
14 Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
He breaketh me with breach upon breach; He runneth upon me like a giant.
15 “Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
I have sewed sackcloth upon my skin, and have laid my horn in the dust.
16 Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
My face is reddened with weeping, and on my eyelids is the shadow of death;
17 komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
Although there is no violence in my hands, and my prayer is pure.
18 “Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
O earth, cover not thou my blood, and let my cry have no resting-place.
19 Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
Even now, behold, my Witness is in heaven, and He that testifieth of me is on high.
20 Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
Mine inward thoughts are my intercessors, mine eye poureth out tears unto God;
21 iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
That He would set aright a man contending with God, as a son of man setteth aright his neighbour!
22 “Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”
For the years that are few are coming on, and I shall go the way whence I shall not return.

< Yobu 16 >