< Yobu 16 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Job replied,
2 “Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
“I've heard all this before. You are comforters who just cause trouble!
3 Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
Will your windy speeches never cease? What's bothering you that you have to answer me?
4 Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
I could talk like you do if you were in my place, stringing words together to criticize you, ridiculing you with a toss of my head.
5 Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
I could build you up by my mouth speaking words; the movement of my lips would ease your pain.
6 “Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
For me, if I speak it doesn't ease my pain, and if I don't speak the pain is still there.
7 Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
God, you have worn me out. You have destroyed my whole family.
8 Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
You have made me shrivel up, which is a witness against me; my thin body testifies against me.
9 Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
He has torn me apart in his anger; in his hostility he has gnashed his teeth at me; my enemy pierces me with his fierce look.
10 Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
People stare at me with their mouths wide open, they slap me on my cheeks to mock me, they crowd around me to attack me.
11 Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
God has handed me over to evil people; he has thrown me into their hands.
12 Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
I was living in peace and he smashed me to pieces. He grabbed me by the neck and dashed me to pieces. He set me up as his target.
13 anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
His archers surround me. His arrows pierce my kidneys without mercy. He pours out my gall on the ground.
14 Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
Like a wall he breaks me down, breach upon breach, rushing at me like a warrior.
15 “Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
I have sown sackcloth to cover my skin; my strength lies broken in the dust.
16 Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
My face is red from crying and dark shadows surround my eyes,
17 komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
although I have done nothing wrong and my prayer is pure.
18 “Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
Earth, do not cover up my blood. May my cry find no place to hide.
19 Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
Look, right now my witness is in heaven; the one who speaks for me is on high.
20 Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
My friends scorn me, but my eyes pour out tears to God.
21 iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
I want my witness to speak for me with God as someone does for their friend.
22 “Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”
For in a few short years I shall go down that road from which I shall not return.