< Yobu 15 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Na Temanni Elifas buaa sɛ,
2 “Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
“Enti onyansafoɔ de nsɛm a aba biara nni muo bɛyi nʼano anaasɛ ɔde apueeɛ mframa a emu yɛ hye bɛhyɛ nʼafuru ma?
3 Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
Ɔde nsɛm huhuo bɛdi anobaabaeɛ, aka nsɛm a ɛntu bunu biara anaa?
4 Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
Wototo onyamesuro ase mmom na wosi Onyankopɔn mu ahotosoɔ ho ɛkwan.
5 Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
Wo bɔne kyerɛ wʼano deɛ ɔnka; na woafa aniteɛ tɛkrɛma.
6 Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
Wo ankasa wʼano bu wo kumfɔ, ɛnyɛ me deɛ; wʼankasa wʼano di adanseɛ tia wo.
7 “Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
“Wone onipa a wɔwoo wo dii ɛkan? Wɔwoo wo ansa na wɔrewo nkokoɔ?
8 Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
Wotie Onyankopɔn afotuo anaa? Wo nko ara na wonim nyansa anaa?
9 Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
Ɛdeɛn na wonim a, yɛnnim? Nhunumu bɛn na wowɔ a yɛnnie?
10 Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
Deɛ wafu dwono ne akɔkoraa wɔ yɛn afa, wɔn a wɔanyini sene wʼagya mpo.
11 Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
Onyankopɔn awerɛkyekyerɛ ne nsɛm a wɔka no brɛoo kyerɛ wo no sua ma wo anaa?
12 Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
Adɛn enti na wʼakoma atwe wo korɔ adɛn enti na wʼani asɔ ogya,
13 moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
na woadane wʼabofuo agu Onyankopɔn so na woma saa nsɛm yi pue firi wʼano?
14 “Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
“Ɔdasani ne hwan a ɔbɛtumi ayɛ pɛ, anaasɛ deɛ ɔbaa awo noɔ bɛn na ɔbɛtumi ayɛ ɔteneneeni?
15 Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
Onyankopɔn nni ahotosoɔ wɔ nʼakronkronfoɔ mu. Ɔsorosoro mpo nnyɛ kronn wɔ nʼani so,
16 nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
na nkantom onipa bɔnefoɔ ne omumuyɛfoɔ a ɔnom awurukasɛm sɛ nsuo.
17 “Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
“Tie me, na mɛkyerɛ wo mu; ma menka deɛ mahunu nkyerɛ wo,
18 zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
deɛ anyansafoɔ apae mu aka, a wɔamfa biribiara a wɔnya firii wɔn agyanom hɔ no ansie
19 (Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
(wɔn a wɔde asase no maa wɔn ɛberɛ a ananafoɔ biara nni hɔ):
20 Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
Omumuyɛfoɔ kɔ ahohiahia mu ne nkwanna nyinaa. Na basabasayɛni nso, wɔahyehyɛ ne mfeɛ nyinaa ama no.
21 Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
Nnyegyeɛ a ɛyɛ hu hyɛ nʼasom ma; na sɛ ɛyɛ sɛ nneɛma rekɔ yie ma no a, akorɔmfoɔ to hyɛ ne so.
22 Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
Ɔpa aba sɛ ɔbɛdwane afiri esum mu; wɔabɔ no ato hɔ ama akofena.
23 Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
Ɔkyinkyini hwehwɛ aduane; ɔnim sɛ esum da no abɛn.
24 Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
Ɔhaw ne ahoyera yi no hu; ɛhyɛ ne so sɛ ɔhene a wasiesie ne ho ama ɔko,
25 chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
ɛfiri sɛ ɔtenetene ne nsa kyerɛ Onyankopɔn na ɔma ne ho so tia Otumfoɔ.
26 Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
Wɔde akokyɛm a emu pi na ɛyɛ den kɔ ne so a wɔnsuro no.
27 “Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
“Ɛwom sɛ sradeɛ ama wɔn afono atotɔ na wɔn asene mu ɛnam agu mmɛbɛ deɛ,
28 munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
nanso wɔbɛtena nkuro a aguo so na wɔatena afie a obi nte mu, afie a ɛrebubu mu.
29 Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
Wɔrenkɔ so nyɛ adefoɔ bio, na wɔn ahonya rennyina, na wɔn agyapadeɛ so bɛte na ayera wɔ asase so.
30 Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
Esum bɛduru wɔn; ogyaframa bɛkusa wɔn mman, na Onyankopɔn anom ahomeguo bɛsoa wɔn akɔ.
31 Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
Ɛnsɛ sɛ wɔde wɔn ho to nneɛma huhuo so de daadaa wɔn ho, ɛfiri sɛ wɔrennya hwee mfiri mu.
32 Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
Ansa na wɔn da bɛduru no, wɔbɛtua wɔn ka a ebi renka, na wɔn mman renyɛ frɔmfrɔm.
33 Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
Wɔbɛyɛ sɛ bobedua a wɔapore so aba a ɛnnyiniiɛ, te sɛ ngo dua a ne nhyerɛnne repore gu fam.
34 Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
Na abɔnefoɔ fekuo a wɔnnim Onyankopɔn no renso aba, na ogya bɛhye wɔn a wɔdɔ kɛtɛasehyɛ no ntomadan.
35 Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”
Wɔnyinsɛn ɔhaw na wɔwo amumuyɛ; wɔn awotwaa siesie nnaadaa.”

< Yobu 15 >