< Yobu 15 >
1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Entonces Elifaz, el temanita, respondió,
2 “Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
“Si un sabio responde con vano conocimiento, y llenarse con el viento del este?
3 Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
Debe razonar con una charla poco provechosa, o con discursos con los que no puede hacer nada bueno?
4 Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
Sí, elimina el miedo, y dificultan la devoción ante Dios.
5 Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
Porque tu iniquidad enseña tu boca, y tú eliges el lenguaje de los astutos.
6 Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
Tu propia boca te condena, y no yo. Sí, tus propios labios testifican contra ti.
7 “Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
“¿Eres tú el primer hombre que nació? ¿O te sacaron antes de las colinas?
8 Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
¿Has oído el consejo secreto de Dios? ¿Limitas la sabiduría a ti mismo?
9 Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
¿Qué sabe usted que nosotros no sepamos? ¿Qué entiendes que no está en nosotros?
10 Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
Con nosotros están tanto los canosos como los muy ancianos, mucho mayor que tu padre.
11 Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
¿Los consuelos de Dios son demasiado pequeños para ti? ¿incluso la palabra que es suave para ti?
12 Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
¿Por qué te arrastra tu corazón? Por qué tus ojos parpadean,
13 moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
que vuelvas tu espíritu contra Dios, y dejar que esas palabras salgan de tu boca?
14 “Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
¿Qué es el hombre, para que esté limpio? ¿Qué es el nacido de mujer, para que sea justo?
15 Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
He aquí que él no confía en sus santos. Sí, los cielos no están limpios a sus ojos;
16 nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
cuánto menos uno que es abominable y corrupto, ¡un hombre que bebe la iniquidad como si fuera agua!
17 “Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
“Te lo mostraré, escúchame; lo que he visto lo declararé
18 zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
(que los sabios han contado por sus padres, y no lo han ocultado;
19 (Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
a quien solo se le dio la tierra, y ningún extraño pasó entre ellos):
20 Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
el malvado se retuerce de dolor todos sus días, incluso el número de años que se le acumulan al opresor.
21 Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
Un sonido de terror está en sus oídos. En la prosperidad el destructor vendrá sobre él.
22 Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
No cree que vaya a volver de las tinieblas. Le espera la espada.
23 Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
Anda por ahí buscando pan, diciendo: “¿Dónde está?”. Sabe que el día de las tinieblas está listo en su mano.
24 Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
La angustia y la angustia le hacen temer. Se imponen contra él, como un rey listo para la batalla.
25 chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
Porque ha extendido su mano contra Dios, y se comporta con orgullo contra el Todopoderoso,
26 Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
corre hacia él con el cuello rígido, con los gruesos escudos de sus rodelas,
27 “Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
porque se ha cubierto la cara con su gordura, y se acumulaba la grasa en los muslos.
28 munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
Ha vivido en ciudades desoladas, en casas que no habitaba nadie, que estaban a punto de convertirse en montones.
29 Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
No será rico, ni su riqueza continuará, ni sus posesiones se extenderán sobre la tierra.
30 Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
No se apartará de las tinieblas. La llama secará sus ramas. Se irá por el soplo de la boca de Dios.
31 Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
Que no confíe en el vacío, engañándose a sí mismo, porque el vacío será su recompensa.
32 Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
Se cumplirá antes de su tiempo. Su rama no será verde.
33 Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
Sacudirá su uva inmadura como la vid, y echará su flor como el olivo.
34 Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
Porque la compañía de los impíos será estéril, y el fuego consumirá las tiendas del soborno.
35 Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”
Conciben el mal y producen la iniquidad. Su corazón prepara el engaño”.