< Yobu 15 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Entonces Elifaz temanita tomó la palabra y dijo:
2 “Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
“¿Es acaso de sabios responder con argumentos vanos, y llenarse el pecho de viento,
3 Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
arguyendo con palabras inútiles, y con razones sin valor?
4 Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
De veras, tú destruyes la piedad y socavas el temor de Dios.
5 Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
Porque tu boca revela tu iniquidad, adoptas el lenguaje de los arteros.
6 Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
Tu propia boca, y no yo, te condena, tus mismos labios testifican contra ti.
7 “Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
¿Naciste tú el primero de los hombres, saliendo a la luz antes que los montes?
8 Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
¿Escuchaste tú los secretos de Dios, secuestraste para ti la sabiduría?
9 Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
¿Qué sabes tú, que no sepamos nosotros? ¿En qué nos supera tu sabiduría?
10 Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
También entre nosotros hay cabezas canas y hombres de edad, más avanzados en días que tu padre.
11 Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
¿Acaso tienes en poco las consolaciones de Dios, y las suaves palabras que se te dicen.
12 Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
¿Adónde te lleva tu corazón, y qué significa el pestañeo de tus ojos?
13 moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
¿Por qué diriges contra Dios tu ira, y profiere tu boca tales palabras?
14 “Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
¿Qué es el hombre para aparecer inocente; el nacido de mujer, para ser justo?
15 Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
Pues Él no se fía ni de sus santos; los mismos cielos no están limpios a su vista;
16 nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
¿cuánto menos este ser, abominable y perverso, el hombre, que bebe como agua la iniquidad?
17 “Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
Te voy a enseñar; escúchame; te voy a contar lo que he visto,
18 zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
lo que los sabios enseñan sin ocultar nada, — (como lo recibieron) de sus padres—
19 (Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
pues a ellos solos fue dado el país, y no pasó extraño alguno entre ellos.
20 Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
Todos sus días el impío es atormentado; y el tirano ignora el número de sus años.
21 Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
Voz de angustia suena en sus oídos; en plena paz le asalta el devastador.
22 Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
Él mismo pierde la esperanza de escapar a las tinieblas; se siente amenazado de la espada;
23 Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
vaga buscando alimento, (diciendo): ¿En dónde está? sabe que es inminente el día de las tinieblas;
24 Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
le aterran angustia y tribulación, le acometen como un rey listo para la guerra.
25 chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
Pues extendió su mano contra Dios, se exaltó contra el Todopoderoso.
26 Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
Corre contra Él, erguido el cuello, ocultándose detrás de sus escudos,
27 “Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
cubierto el rostro con su gordura, con capas de grosura sus lomos.
28 munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
Vive en ciudades asoladas, en casas inhabitadas, destinadas a convertirse en ruinas.
29 Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
Por eso no será rico, sus bienes no durarán, y su hacienda no se extenderá sobre la tierra.
30 Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
Nunca escapará a las tinieblas; la llama abrasará sus renuevos, y él será llevado por el soplo de la boca de (Dios).
31 Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
No confíe en una engañosa vanidad; la misma vanidad será su recompensa.
32 Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
Ella le llegará antes que se acaben sus días, y sus ramas no reverdecerán ya más.
33 Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
Sacudirá como la vid sus uvas, aun estando en cierne, y como el olivo dejará caer su flor.
34 Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
La casa del impío es estéril, y el fuego consume la morada del que se deja sobornar.
35 Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”
Concibe penas y engendra maldades, nutriendo en su seno el engaño.”

< Yobu 15 >