< Yobu 15 >
1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Então respondeu Eliphaz o themanita, e disse:
2 “Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
Porventura dará o sabio por resposta sciencia de vento? e encherá o seu ventre de vento oriental?
3 Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
Arguindo com palavras que de nada servem e com razões, com que nada aproveita?
4 Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
E tu tens feito vão o temor, e diminues os rogos diante de Deus.
5 Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
Porque a tua bocca declara a tua iniquidade; e tu escolheste a lingua dos astutos.
6 Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
A tua bocca te condemna, e não eu, e os teus labios testificam contra ti.
7 “Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
És tu porventura o primeiro homem que foi nascido? ou foste gerado antes dos outeiros?
8 Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
Ou ouviste o secreto conselho de Deus? e a ti só limitaste a sabedoria?
9 Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
Que sabes tu, que nós não sabemos? e que entendes, que não haja em nós?
10 Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
Tambem ha entre nós encanecidos e edosos, muito mais edosos do que teu pae.
11 Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
Porventura as consolações de Deus te são pequenas? ou alguma coisa se occulta em ti
12 Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
Porque te arrebata o teu coração? e porque acenam os teus olhos?
13 moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
Para virares contra Deus o teu espirito, e deixares sair taes palavras da tua bocca?
14 “Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
Que é o homem, para que seja puro? e o que nasce da mulher, para que fique justo?
15 Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
Eis que nos seus sanctos não confiaria, e nem os céus são puros aos seus olhos.
16 nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
Quanto mais abominavel e fedorento é o homem que bebe a iniquidade como a agua?
17 “Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
Escuta-me, mostrar-t'o-hei: e o que vi te contarei
18 zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
(O que os sabios annunciaram, ouvindo-o de seus paes, e o não occultaram.
19 (Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
Aos quaes sómente se déra a terra, e nenhum estranho passou por meis d'elles):
20 Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
Todos os dias o impio se dá pena a si mesmo, e se reservam para o tyranno um certo numero d'annos.
21 Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
O sonido dos horrores está nos seus ouvidos: até na paz lhe sobrevem o assolador.
22 Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
Não crê que tornará das trevas, e que está esperado da espada.
23 Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
Anda vagueando por pão, dizendo: Onde está? Bem sabe que já o dia das trevas lhe está preparado á mão.
24 Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
Assombram-n'o a angustia e a tribulação; prevalecem contra elle, como o rei preparado para a peleja.
25 chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
Porque estende a sua mão contra Deus, e contra o Todo-poderoso se embravece.
26 Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
Arremette contra elle com a dura cerviz, e contra os pontos grossos dos seus escudos.
27 “Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
Porquanto cobriu o seu rosto com a sua gordura, e criou enxundia nas ilhargas.
28 munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
E habitou em cidades assoladas, em casas em que ninguem morava, que estavam a ponto de fazer-se montões de ruinas.
29 Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
Não se enriquecerá, nem subsistirá a sua fazenda, nem se estenderão pela terra as suas possessões.
30 Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
Não escapará das trevas; a chamma do fogo seccará os seus renovos, e ao assopro da sua bocca desapparecerá.
31 Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
Não confie pois na vaidade enganando-se a si mesmo, porque a vaidade será a sua recompensa.
32 Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
Antes do seu dia ella se lhe cumprirá; e o seu ramo não reverdecerá.
33 Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
Sacudirá as suas uvas verdes, como as da vide, e deixará cair a sua flor como a da oliveira.
34 Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
Porque o ajuntamento dos hypocritas se fará esteril, e o fogo consumirá as tendas do soborno.
35 Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”
Concebem o trabalho, e parem a iniquidade, e o seu ventre prepara enganos.