< Yobu 15 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Respondens autem Eliphaz Themanites, dixit:
2 “Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
Numquid sapiens respondebit quasi in ventum loquens, et implebit ardore stomachum suum?
3 Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
Arguis verbis eum, qui non est aequalis tibi, et loqueris quod tibi non expedit.
4 Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
Quantum in te est evacuasti timorem, et tulisti preces coram Deo.
5 Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
Docuit enim iniquitas tua os tuum, et imitaris linguam blasphemantium.
6 Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
Condemnabit te os tuum, et non ego: et labia tua respondebunt tibi.
7 “Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
Numquid primus homo tu natus es, et ante colles formatus?
8 Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
Numquid consilium Dei audisti, et inferior te erit eius sapientia?
9 Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
Quid nosti quod ignoremus? quid intelligis quod nesciamus?
10 Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
Et senes, et antiqui sunt in nobis multo vetustiores quam patres tui.
11 Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
Numquid grande est ut consoletur te Deus? sed verba tua prava hoc prohibent
12 Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
Quid te elevat cor tuum, et quasi magna cogitans, attonitos habes oculos?
13 moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
Quid tumet contra Deum spiritus tuus, ut proferas de ore tuo huiuscemodi sermones?
14 “Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
Quid est homo, ut immaculatus sit, et ut iustus appareat natus de muliere?
15 Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
Ecce inter sanctos eius nemo immutabilis, et caeli non sunt mundi in conspectu eius.
16 nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
Quanto magis abominabilis et inutilis homo, qui bibit quasi aquam iniquitatem?
17 “Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
Ostendam tibi, audi me: quod vidi narrabo tibi.
18 zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
Sapientes confitentur, et non abscondunt patres suos.
19 (Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
Quibus solis data est terra, et non transivit alienus per eos.
20 Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
Cunctis diebus suis impius superbit, et numerus annorum incertus est tyrannidis eius.
21 Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
Sonitus terroris semper in auribus illius: et cum pax sit, ille semper insidias suspicatur.
22 Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
Non credit quod reverti possit de tenebris ad lucem, circumspectans undique gladium.
23 Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
Cum se moverit ad quaerendum panem, novit quod paratus sit in manu eius tenebrarum dies.
24 Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
Terrebit eum tribulatio, et angustia vallabit eum, sicut regem, qui praeparatur ad praelium.
25 chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
Tetendit enim adversus Deum manum suam, et contra Omnipotentem roboratus est.
26 Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
Cucurrit adversus eum erecto collo, et pingui cervice armatus est.
27 “Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
Operuit faciem eius crassitudo, et de lateribus eius arvina dependet.
28 munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
Habitavit in civitatibus desolatis, et in domibus desertis, quae in tumulos sunt redactae.
29 Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
Non ditabitur, nec perseverabit substantia eius, nec mittet in terra radicem suam.
30 Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
Non recedet de tenebris: ramos eius arefaciet flamma, et auferetur spiritu oris sui.
31 Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
Non credet frustra errore deceptus, quod aliquo pretio redimendus sit.
32 Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
Antequam dies eius impleantur, peribit: et manus eius arescent.
33 Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
Laedetur quasi vinea in primo flore botrus eius, et quasi oliva proiiciens florem suum.
34 Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
Congregatio enim hypocritae sterilis, et et ignis devorabit tabernacula eorum, qui munera libenter accipiunt.
35 Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”
Concepit dolorem, et peperit iniquitatem, et uterus eius praeparat dolos.

< Yobu 15 >