< Yobu 15 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
テマン人エリパズ答へて曰く
2 “Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
智者あに虚しき智識をもて答へんや豈東風をその腹に充さんや
3 Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
あに裨なき談益なき詞をもて辨論はんや
4 Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
まことに汝は神を畏るる事を棄て その前に祷ることを止む
5 Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
なんぢの罪なんぢの口を教ふ 汝はみづから擇びて狡猾人の舌を用ふ
6 Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
なんぢの口みづから汝の罪を定む 我には非ず汝の唇なんぢの惡きを證す
7 “Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
汝あに最初に世に生れたる人ならんや 山よりも前に出來しならんや
8 Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
神の御謀議を聞しならんや 智慧を獨にて藏めをらんや
9 Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
なんぢが知る所は我らも知ざらんや 汝が曉るところは我らの心にも在ざらんや
10 Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
我らの中には白髮の人および老たる人ありて汝の父よりも年高し
11 Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
神の慰藉および夫の柔かき言詞を汝小しとするや
12 Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
なんぢ何ぞかく心狂ふや 何ぞかく目をしばたたくや
13 moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
なんぢ是のごとく神に對ひて氣をいらだて 斯る言詞をなんぢの口よりいだすは如何ぞや
14 “Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
人は如何なる者ぞ 如何してか潔からん 婦の産し者は如何なる者ぞ 如何してか義からん
15 Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
それ神はその聖者にすら信を置たまはず 諸の天もその目の前には潔からざるなり
16 nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
況んや罪を取ること水を飮が如くする憎むべき穢れたる人をや
17 “Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
我なんぢに語る所あらん 聽よ我見たる所を述ん
18 zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
是すなはち智者等が父祖より受て隱すところなく傳へ來し者なり
19 (Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
彼らに而已この地は授けられて外國人は彼等の中に往來せしこと無りき
20 Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
惡き人はその生る日の間つねに悶へ苦しむ 強暴人の年は數へて定めおかる
21 Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
その耳には常に懼怖しき音きこえ平安の時にも滅ぼす者これに臨む
22 Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
彼は幽暗を出得るとは信ぜず 目ざされて劒に付さる
23 Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
彼食物は何處にありやと言つつ尋ねありき 黒暗日の備へられて己の側にあるを知る
24 Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
患難と苦痛とはかれを懼れしめ 戰鬪の準備をなせる王のごとくして彼に打勝ん
25 chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
彼は手を伸て神に敵し 傲りて全能者に悖り
26 Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
頸を強くし 厚き楯の面を向て之に馳かかり
27 “Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
面に肉を滿せ 腰に脂を凝し
28 munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
荒されたる邑々に住居を設けて人の住べからざる家 石堆となるべき所に居る
29 Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
是故に彼は富ず その貨物は永く保たず その所有物は地に蔓延ず
30 Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
また自己は黒暗を出づるに至らず 火燄その枝葉を枯さん 而してその身は神の口の氣吹によりて亡ゆかん
31 Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
彼は虚妄を恃みて自ら欺くべからず 其報は虚妄なるべければなり
32 Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
彼の日の來らざる先に其事成べし 彼の枝は緑ならじ
33 Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
彼は葡萄の樹のその熟せざる果を振落すがごとく 橄欖の樹のその花を落すがごとくなるべし
34 Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
邪曲なる者の宗族は零落れ 賄賂の家は火に焚ん
35 Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”
彼等は惡念を孕み 虚妄を生み その胎にて詭計を調ふ

< Yobu 15 >