< Yobu 15 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Eliphaz de Têmân prit la parole et dit:
2 “Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
Est-il digne du sage de mettre en avant des raisons futiles, de gonfler son sein de vent?
3 Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
d’employer des arguments sans valeur et des paroles qui ne servent de rien?
4 Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
Tu en viens à saper la piété, à supprimer les prières au Tout-Puissant!
5 Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
C’Est ton iniquité qui inspire ta bouche, et ainsi tu adoptes le langage de la mauvaise foi.
6 Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
C’Est ta bouche qui te condamne, et non moi; tes propres lèvres témoignent contre toi.
7 “Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
Es-tu donc, par ta naissance, le premier des hommes? As-tu vu le jour avant les collines?
8 Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
As-tu entendu ce qui se dit dans le conseil de Dieu? As-tu confisqué à ton profit la sagesse?
9 Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
Que sais-tu que nous ne sachions? Que comprends-tu qui nous échappe?
10 Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
Parmi nous aussi il est des gens vénérables par l’âge, des vieillards plus riches de jours que ton père.
11 Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
Comptes-tu pour rien les consolations de Dieu et la parole qui t’a été dite en douceur?
12 Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
Pourquoi te laisser emporter par ton cœur? Pourquoi rouler ainsi tes yeux?
13 moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
Pourquoi tourner ta mauvaise humeur contre Dieu et laisser échapper de tels discours de ta bouche?
14 “Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
Qu’est-ce donc que l’homme pour se prétendre pur et l’enfant de la femme pour se dire juste?
15 Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
Quoi! Même en ses saints il n’a pas confiance, et les cieux ne sont pas sans tache à ses yeux!
16 nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
Que sera-ce de cet être méprisable et corrompu, de l’homme qui boit l’iniquité comme l’eau?
17 “Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
Je veux t’instruire, écoute-moi; je veux t’exposer ce que j’ai vu;
18 zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
ce que racontent les sages, sans rien dissimuler, comme une tradition de leurs pères,
19 (Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
qui furent, seuls, maîtres de ce pays et auxquels nul étranger ne s’est mêlé:
20 Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
"Les tourments remplissent toute la vie du méchant, tout le cours des années mesurées au tyran.
21 Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
Ses oreilles ne cessent d’entendre un bruit terrifiant; en pleine paix, il se voit assaillir par le dévastateur.
22 Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
Il renonce à l’espoir d’échapper aux ténèbres, il se sait prédestiné au glaive.
23 Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
Il erre ça et là pour chercher du pain: il a conscience que des jours sombres se préparent pour lui.
24 Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
La détresse et l’angoisse le jettent dans l’épouvante; elles l’étreignent comme un roi qui monte à l’assaut.
25 chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
C’Est qu’il a dirigé sa main contre Dieu, il s’est élevé contre le Tout-Puissant.
26 Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
C’Est qu’il lui a couru sus, le cou tendu, couvert de toute l’épaisseur de ses boucliers bombés.
27 “Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
C’Est qu’il a le visage épaissi par la graisse et le dos arrondi par l’embonpoint.
28 munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
Aussi se fixe-t-il dans des villes en ruines, dans des maisons qui ne sont pas habitables, étant destinées à se changer en décombres.
29 Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
Il ne s’enrichira pas, sa fortune ne subsistera point; tel un arbre sans fruits il n’inclinera pas à terre le sommet de ses branches.
30 Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
Il ne sortira plus des ténèbres; ses rejetons seront consumés par le feu; il disparaîtra comme par un souffle de Dieu.
31 Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
Qu’il n’espère rien de la fraude! II a fait fausse route. La déception sera son salaire.
32 Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
Sa carrière sera achevée avant le temps, et son toit de feuillage ne reverdira plus.
33 Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
Tel qu’une vigne, il sera dépouillé de ses jeunes grappes; tel qu’un olivier, il jettera ses fleurs.
34 Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
Car la bande des pervers est condamnée à la stérilité; le feu dévore les tentes où s’entassent les dons de la corruption.
35 Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”
Ils conçoivent le mal, ils enfantent le malheur. Leur sein couve la perfidie.

< Yobu 15 >