< Yobu 15 >
1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Forsothe Eliphat Themanytes answeride, and seide,
2 “Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
Whether a wise man schal answere, as spekynge ayens the wynd, and schal fille his stomac with brennyng, `that is, ire?
3 Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
For thou repreuest hym bi wordis, which is not lijk thee, and thou spekist that, that spedith not to thee.
4 Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
As myche as is in thee, thou hast avoidid drede; and thou hast take awey preyeris bifor God.
5 Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
For wickidnesse hath tauyt thi mouth, and thou suest the tunge of blasfemeris.
6 Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
Thi tunge, and not Y, schal condempne thee, and thi lippis schulen answere thee.
7 “Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
Whether thou art borun the firste man, and art formed bifor alle little hillis?
8 Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
Whether thou herdist the counsel of God, and his wisdom is lower than thou?
9 Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
What thing knowist thou, whiche we knowen not? What thing vndurstondist thou, whiche we witen not?
10 Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
Bothe wise men and elde, myche eldre than thi fadris, ben among vs.
11 Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
Whether it is greet, that God coumforte thee? But thi schrewid wordis forbeden this.
12 Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
What reisith thin herte thee, and thou as thenkynge grete thingis hast iyen astonyed?
13 moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
What bolneth thi spirit ayens God, that thou brynge forth of thi mouth siche wordis?
14 “Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
What is a man, that he be with out wem, and that he borun of a womman appere iust?
15 Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
Lo! noon among hise seyntis is vnchaungable, and heuenes ben not cleene in his siyt.
16 nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
How myche more a man abhomynable and vnprofitable, that drynkith wickidnesse as water?
17 “Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
I schal schewe to thee, here thou me; Y schal telle to thee that, that Y siy.
18 zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
Wise men knoulechen, and hiden not her fadris.
19 (Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
To whiche aloone the erthe is youun, and an alien schal not passe bi hem.
20 Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
A wickid man is proud in alle hise daies; and the noumbre of hise yeeris and of his tirauntrie is vncerteyn.
21 Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
The sown of drede is euere in hise eeris, and whanne pees is, he supposith euere tresouns.
22 Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
He bileueth not that he may turne ayen fro derknessis to liyt; and biholdith aboute on ech side a swerd.
23 Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
Whanne he stirith hym to seke breed, he woot, that the dai of derknessis is maad redi in his hond.
24 Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
Tribulacioun schal make hym aferd, and angwisch schal cumpas hym, as a kyng which is maad redi to batel.
25 chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
For he helde forth his hond ayens God, and he was maad strong ayens Almyyti God.
26 Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
He ran with neck reisid ayens God, and he was armed with fat nol.
27 “Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
Fatnesse, that is, pride `comyng forth of temporal aboundaunce, hilide his face, `that is, the knowyng of vndurstondyng, and outward fatnesse hangith doun of his sidis.
28 munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
He schal dwelle in desolat citees, and in deseert, `ethir forsakun, housis, that ben turned in to biriels.
29 Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
He schal not be maad riche, nether his catel schal dwelle stidefastli; nether he schal sende his roote in the erthe,
30 Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
nether he schal go awei fro derknessis. Flawme schal make drie hise braunchis, and he schal be takun a wey bi the spirit of his mouth.
31 Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
Bileue he not veynli disseyued bi errour, that he schal be ayenbouyt bi ony prijs.
32 Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
Bifor that hise daies ben fillid, he schal perische, and hise hondis schulen wexe drye;
33 Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
he schal be hirt as a vyne in the firste flour of his grape, and as an olyue tre castinge awei his flour.
34 Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
For the gaderyng togidere of an ipocrite is bareyn, and fier schal deuoure the tabernaclis of hem, that taken yiftis wilfuli.
35 Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”
He conseyuede sorewe, and childide wickidnesse, and his wombe makith redi tretcheries.