< Yobu 15 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
And Eliphaz the Temanite answers and says:
2 “Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
“Does a wise man answer [with] vain knowledge? And fill his belly [with] an east wind?
3 Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
To reason with a word not useful? And speeches—no profit in them?
4 Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
Indeed, you make reverence void, and diminish meditation before God.
5 Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
For your mouth teaches your iniquity, And you choose the tongue of the cunning.
6 Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
Your mouth declares you wicked, and not I, And your lips testify against you.
7 “Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
Are you the first man born? And were you formed before the heights?
8 Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
Do you hear of the secret counsel of God? And withdraw wisdom to you?
9 Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
What have you known, and we do not know? [What] do you understand, and it is not with us?
10 Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
Both the gray-headed And the very aged [are] among us—Greater than your father [in] days.
11 Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
Are the comforts of God too few for you? And a gentle word [is] with you,
12 Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
Why does your heart take you away? And why are your eyes high?
13 moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
Do you turn your spirit against God? And have brought out words from your mouth:
14 “Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
What [is] man that he is pure, And that he is righteous, one born of woman?
15 Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
Behold, He puts no credence in His holy ones, And the heavens have not been pure in His eyes.
16 nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
Also—surely abominable and filthy Is man drinking perverseness as water.
17 “Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
I show you—listen to me—And this I have seen and declare,
18 zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
Which the wise declare—And have not hid—from their fathers.
19 (Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
To them alone was the land given, And a stranger did not pass over into their midst:
20 Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
All [the] days of the wicked he is paining himself, And few years have been laid up for the terrible one.
21 Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
A fearful voice [is] in his ears, In peace a destroyer comes to him.
22 Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
He does not believe to return from darkness, And he watches for the sword.
23 Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
He is wandering for bread: Where [is] it? He has known that ready at his hand Is a day of darkness.
24 Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
Adversity and distress terrify him, They prevail over him as a king ready for a boaster.
25 chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
For he stretched out his hand against God, And against the Mighty he makes himself mighty.
26 Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
He runs to Him with a neck, With thick bosses of his shields.
27 “Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
For he has covered his face with his fat, And makes vigor over [his] confidence.
28 munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
And he inhabits cities cut off, houses not dwelt in, That have been ready to become heaps.
29 Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
He is not rich, nor does his wealth rise, Nor does he stretch out their continuance on earth.
30 Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
He does not turn aside from darkness, A flame dries up his tender branch, And he turns aside at the breath of His mouth!
31 Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
Do not let him put credence in vanity, He has been deceived, For vanity is his exchange.
32 Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
It is not completed in his day, And his bending branch is not green.
33 Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
He shakes off his unripe fruit as a vine, And casts off his blossom as an olive.
34 Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
For the company of the profane [is] barren, And fire has consumed tents of bribery.
35 Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”
To conceive misery, and to bear iniquity, Even their heart prepares deceit.”

< Yobu 15 >