< Yobu 15 >
1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Then answered Eliphaz the Temanite, and said,
2 “Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
Should a wise man utter vain knowledge, and fill his belly with the east wind?
3 Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
Should he reason with unprofitable talk? or with speeches wherewith he can do no good?
4 Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
Yea, thou castest off fear, and restrainest prayer before God.
5 Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
For thy mouth uttereth thine iniquity, and thou choosest the tongue of the crafty.
6 Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
Thine own mouth condemneth thee, and not I: yea, thine own lips testify against thee.
7 “Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
[Art] thou the first man [that] was born? or wast thou made before the hills?
8 Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
Hast thou heard the secret of God? and dost thou restrain wisdom to thyself?
9 Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
What knowest thou, that we know not? [what] understandest thou, which [is] not in us?
10 Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
With us [are] both the grayheaded and very aged men, much elder than thy father.
11 Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
[Are] the consolations of God small with thee? is there any secret thing with thee?
12 Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
Why doth thine heart carry thee away? and what do thy eyes wink at,
13 moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
That thou turnest thy spirit against God, and lettest [such] words go out of thy mouth?
14 “Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
What [is] man, that he should be clean? and [he which is] born of a woman, that he should be righteous?
15 Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
Behold, he putteth no trust in his saints; yea, the heavens are not clean in his sight.
16 nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
How much more abominable and filthy [is] man, which drinketh iniquity like water?
17 “Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
I will shew thee, hear me; and that [which] I have seen I will declare;
18 zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
Which wise men have told from their fathers, and have not hid [it: ]
19 (Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
Unto whom alone the earth was given, and no stranger passed among them.
20 Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
The wicked man travaileth with pain all [his] days, and the number of years is hidden to the oppressor.
21 Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
A dreadful sound [is] in his ears: in prosperity the destroyer shall come upon him.
22 Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
He believeth not that he shall return out of darkness, and he is waited for of the sword.
23 Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
He wandereth abroad for bread, [saying], Where [is it]? he knoweth that the day of darkness is ready at his hand.
24 Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
Trouble and anguish shall make him afraid; they shall prevail against him, as a king ready to the battle.
25 chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
For he stretcheth out his hand against God, and strengtheneth himself against the Almighty.
26 Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
He runneth upon him, [even] on [his] neck, upon the thick bosses of his bucklers:
27 “Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
Because he covereth his face with his fatness, and maketh collops of fat on [his] flanks.
28 munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
And he dwelleth in desolate cities, [and] in houses which no man inhabiteth, which are ready to become heaps.
29 Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
He shall not be rich, neither shall his substance continue, neither shall he prolong the perfection thereof upon the earth.
30 Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
He shall not depart out of darkness; the flame shall dry up his branches, and by the breath of his mouth shall he go away.
31 Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
Let not him that is deceived trust in vanity: for vanity shall be his recompence.
32 Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
It shall be accomplished before his time, and his branch shall not be green.
33 Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
He shall shake off his unripe grape as the vine, and shall cast off his flower as the olive.
34 Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
For the congregation of hypocrites [shall be] desolate, and fire shall consume the tabernacles of bribery.
35 Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”
They conceive mischief, and bring forth vanity, and their belly prepareth deceit.