< Yobu 15 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
But Eliphaz the Themanite, answering, said:
2 “Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
Will a wise man answer as if he were speaking wind, and will he fill his stomach with fire?
3 Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
You rebuke with words he who is not equal to you, and you speak what is not expedient for you,
4 Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
to such an extent that, within yourself, you have expelled reverence and have taken away prayers from the presence of God.
5 Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
For your iniquity has mislead your mouth, and you imitate the tongue of blasphemers.
6 Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
Your own mouth will condemn you, not I; and your own lips will answer you.
7 “Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
Are you the first man who was born, or were you formed before the hills?
8 Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
Have you heard the intentions of God, and will his wisdom be inferior to you?
9 Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
What do you know, about which we are ignorant? What do you understand that we do not know?
10 Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
There are with us both aged and ancient men, even more senior than your fathers.
11 Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
Is it so important that God should console you? But your own depraved words prevent this.
12 Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
Why does your heart exalt you, and why do you gaze with your eyes, as if thinking great things?
13 moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
Why does your spirit stir against God, so as to utter such speeches from your mouth?
14 “Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
What is man that he should be immaculate, and that he should appear just, having been born of woman?
15 Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
Behold, among his holy ones not one is immutable, and even the heavens are not pure in his sight.
16 nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
How much more abominable and useless is the man who drinks as if from the water of iniquity?
17 “Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
I will reveal to you, so listen to me; and I will explain to you what I have seen.
18 zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
The wise acknowledge, and they do not leave behind, their fathers,
19 (Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
to whom alone the earth has been given, and no stranger passed among them.
20 Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
The impious is arrogant for all his days, and the number of the years of his tyranny is uncertain.
21 Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
The sound of terror is always in his ears; and when there is peace, he always suspects treason.
22 Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
He does not believe that it is possible for him to be turned from darkness into the light, for he sees around him the sword on every side.
23 Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
When he moves himself to seek bread, he knows that the day of darkness has been prepared for his hand.
24 Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
Tribulation will terrify him, and anguish will prevail over him, like a king who is being prepared to go to battle.
25 chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
For he has extended his hand against God, and he has strengthened himself against the Almighty.
26 Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
He has rushed against him with his throat exposed, and he has been armed with a fat neck.
27 “Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
Thickness has covered his face, and lard hangs down from his sides.
28 munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
He has lived in desolate cities and deserted houses, which have been turned into tombs.
29 Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
He will not be enriched, nor will his basic necessities endure, nor will he establish his root in the earth.
30 Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
He will not withdraw from the darkness; the flame will burn up his branches, and he will be defeated by the breath of his own mouth.
31 Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
He will not believe, being vainly deceived by error, that he could be redeemed at any price.
32 Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
Before his time is completed, he will pass into ruin and his hands will wither away.
33 Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
He will be wounded like a grapevine, when its cluster is in first flower, and like an olive tree that casts off its flower.
34 Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
For the congregation of the hypocrites is fruitless, and fire will devour the tabernacles of those who love to accept money.
35 Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”
He has conceived sorrow, and he has brought forth iniquity, and his womb prepares deceit.

< Yobu 15 >