< Yobu 15 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Så tog Temaniten Elifaz til Orde og sagde:
2 “Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
"Mon Vismand svarer med Mundsvejr og fylder sit Indre med Østenvind
3 Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
for at hævde sin Ret med gavnløs Tale, med Ord, som intet båder?
4 Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
Desuden nedbryder du Gudsfrygt og krænker den Stilhed, som tilkommer Gud.
5 Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
Din Skyld oplærer din Mund, du vælger de listiges Sprog.
6 Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
Din Mund domfælder dig, ikke jeg, dine Læber vidner imod dig!
7 “Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
Var du den første, der fødtes, kom du til Verden, før Højene var?
8 Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
Mon du lytted til, da Gud holdt Råd, og mon du rev Visdommen til dig?
9 Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
Hvad ved du, som vi ikke ved, hvad forstår du, som vi ikke kender?
10 Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
Også vi har en gammel iblandt os, en Olding, hvis Dage er fler end din Faders!
11 Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
Er Guds Trøst dig for lidt, det Ord, han mildelig talede til dig?
12 Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
Hvi river dit Hjerte dig hen, hvi ruller dit Øje vildt?
13 moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
Thi du vender din Harme mod Gud og udstøder Ord af din Mund.
14 “Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
Hvor kan et Menneske være rent, en kvindefødt have Ret?
15 Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
End ikke sine Hellige tror han, og Himlen er ikke ren i hans Øjne,
16 nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
hvad da den stygge, den onde, Manden, der drikker Uret som Vand!
17 “Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
Jeg vil sige dig noget, hør mig, jeg fortæller, hvad jeg har set,
18 zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
hvad vise Mænd har forkyndt, deres Fædre ikke dulgt,
19 (Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
dem alene var Landet givet, ingen fremmed færdedes blandt dem:
20 Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
Den gudløse ængstes hele sit Liv, de stakkede År, en Voldsmand lever;
21 Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
Rædselslyde fylder hans Ører, midt under Fred er Hærgeren over ham;
22 Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
han undkommer ikke fra Mørket, opsparet er han for Sværdet,
23 Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
udset til Føde for Gribbe, han ved, at han står for Fald;
24 Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
Mørkets Dag vil skræmme ham. Trængsel og Angst overvælde ham som en Konge, rustet til Strid.
25 chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
Thi Hånden rakte han ud mod Gud og bød den Almægtige Trods,
26 Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
stormed bårdnakket mod ham med sine tykke, buede Skjolde.
27 “Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
Thi han dækked sit Ansigt med Fedt og samlede Huld på sin Lænd.
28 munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
tog Bolig i Byer, der øde lå hen. i Huse, man ikke må bo i, bestemt til at ligge i Grus.
29 Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
Han bliver ej rig, hans Velstand forgår, til Jorden bøjer sig ikke hans Aks;
30 Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
han undkommer ikke fra Mørket. Solglød udtørrer hans Spire, hans Blomst rives bort af Vinden.
31 Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
Han stole ikke på Tomhed han farer vild thi Tomhed skal være hans Løn!
32 Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
I Utide visner hans Stamme, hans Palmegren skal ikke grønnes;
33 Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
han ryster som Ranken sin brue af og kaster som Olietræet sin Blomst.
34 Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
Thi vanhelliges Samfund er goldt, og Ild fortærer Bestikkelsens Telte;
35 Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”
svangre med Kvide, føder de Uret, og deres Moderskød fostrer Svig!

< Yobu 15 >