< Yobu 15 >

1 Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
Tedy odpovídaje Elifaz Temanský, řekl:
2 “Kodi munthu wanzeru angayankhe ndi mawu achabechabe otere, kapena angakhutitse mimba yake ndi mphepo yotentha yochokera kummawa?
Zdali moudrý vynášeti má umění povětrné, aneb naplňovati východním větrem břicho své,
3 Kodi angathe kutsutsa ndi mawu opanda pake, kapena kuyankhula mawu opanda phindu?
Hádaje se slovy neprospěšnými, aneb řečmi neužitečnými?
4 Koma iwe ukuchepetsa zoopa Mulungu ndipo ukutchinga zodzikhuthulira kwa Mulungu.
Anobrž vyprazdňuješ i bázeň Boží, a modliteb k Bohu činiti se zbraňuješ.
5 Tchimo lako ndiye likuyankhulitsa pakamwa pakopo; ndipo watengera mayankhulidwe a atambwali.
Osvědčujíť zajisté nepravost tvou ústa tvá, ač jsi koli sobě zvolil jazyk chytrých.
6 Pakamwa pakopo ndiye pakukutsutsa osati pakamwa panga; milomo yakoyo ikukutsutsa.
Potupují tě ústa tvá, a ne já, a rtové tvoji svědčí proti tobě.
7 “Kodi ndiwe munthu woyamba kubadwa? Kodi unalengedwa mapiri asanalengedwe?
Zdaliž ty nejprv z lidí zplozen jsi, aneb prvé než pahrbkové sformován?
8 Kodi unali mʼgulu la alangizi a Mulungu? Kodi ukudziyesa wanzeru ndiwe wekha?
Zdaliž jsi tajemství Boží slyšel, že u sebe zavíráš moudrost?
9 Kodi iwe umadziwa chiyani chimene ife sitichidziwa? Kodi iwe uli ndi chidziwitso chanji chimene ife tilibe?
Co víš, čehož bychom nevěděli? Čemu rozumíš, aby toho při nás nebylo?
10 Anthu a imvi ndi okalamba ali mbali yathu, anthu amvulazakale kupambana abambo ako.
I šedivýť i stařec mezi námi jest, ano i starší věkem než otec tvůj.
11 Kodi mawu otonthoza mtima ochokera kwa Mulungu sakukukwanira, mawu oyankhula mofatsawa kwa iwe?
Zdali malá jsou tobě potěšování Boha silného, čili něco je zastěňuje tobě?
12 Chifukwa chiyani ukupsa mtima, ndipo chifukwa chiyani ukutuzula maso ako,
Tak-liž tě jalo srdce tvé, a tak-liž blíkají oči tvé,
13 moti ukupsera mtima Mulungu ndi kuyankhula mawu otero pakamwa pako?
Že smíš odpovídati Bohu silnému tak pyšně, a vypouštěti z úst svých ty řeči?
14 “Kodi munthu nʼchiyani kuti nʼkukhala woyera mtima kapena wobadwa mwa amayi nʼchiyani kuti nʼkukhala wolungama mtima?
Nebo což jest člověk, aby se mohl očistiti, aneb spravedliv býti narozený z ženy?
15 Ngati Mulungu sakhulupirira ngakhale angelo ake, ngakhale zakumwamba sizoyera pamaso pake,
An při svatých jeho není dokonalosti, a nebesa nejsou čistá před očima jeho,
16 nanga kuli bwanji munthu amene ndi wonyansa ndi wa njira zokhotakhota, amene kuchita zoyipa kuli ngati kumwa madzi.
Nadto ohavný a neužitečný člověk, kterýž pije nepravost jako vodu.
17 “Mvetsera kwa ine ndipo ndidzakufotokozera; ndilole ndikuwuze zimene ndaziona,
Já oznámím tobě, poslyš mne; to zajisté, což jsem viděl, vypravovati budu,
18 zimene anandiphunzitsa anthu anzeru, sanandibisire kalikonse kamene anamva kuchokera kwa makolo awo.
Což moudří vynesli a nezatajili, slýchavše od předků svých.
19 (Ndi kwa iwowa kumene dziko lino linaperekedwa pamene panalibe mlendo wokhala pakati pawo).
Jimž samým dána byla země, aniž přejíti mohl cizí prostředkem jejich.
20 Munthu woyipa amavutika ndi masautso masiku onse a moyo wake, munthu wankhanza adzavutika zaka zake zonse.
Po všecky své dny bezbožný sám se bolestí trápí, po všecka, pravím léta, skrytá před ukrutníkem.
21 Amamva mawu owopsa mʼmakutu mwake, pamene zonse zikuoneka ngati zili bwino, anthu achifwamba amamuthira nkhondo.
Zvuk strachu jest v uších jeho, že i v čas pokoje zhoubce připadne na něj.
22 Iye sakhulupirira kuti angathe kupulumuka ku mdima wa imfa; iyeyo ndi woyenera kuphedwa.
Nevěří, by se měl navrátiti z temností, ustavičně očekávaje na sebe meče.
23 Amangoyendayenda pali ponse kunka nafuna chakudya; amadziwa kuti tsiku la mdima lili pafupi.
Bývá i tulákem, chleba hledaje, kde by byl, cítě, že pro něj nastrojen jest den temností.
24 Masautso ndi nthumanzi zimamuchititsa mantha kwambiri; zimamugonjetsa iye monga imachitira mfumu yokonzekera kukathira nkhondo,
Děsí jej nátisk a ssoužení, kteréž se silí proti němu, jako král s vojskem sšikovaným.
25 chifukwa iye amatambasula dzanja lake kuyambana ndi Mulungu ndipo amadzitama yekha polimbana ndi Wamphamvuzonse.
Nebo vztáhl proti Bohu silnému ruku svou, a proti Všemohoucímu postavil se.
26 Amapita mwa mwano kukalimbana naye atanyamula chishango chochindikala ndi cholimba.
Útok učinil na něj, na šíji jeho s množstvím zdvižených štítů svých.
27 “Ngakhale nkhope yake ndi yonenepa ndipo mʼchiwuno mwake muli mnofu wambiri,
Nebo přiodíl tvář svou tukem svým, tak že se mu nadělalo faldů na slabinách.
28 munthuyo adzakhala mʼmizinda yowonongeka ndi mʼnyumba zosayenera kukhalamo anthu, nyumba zimene zikugwa ndi kuwonongeka.
A bydlil v městech zkažených, a v domích, v nichž žádný nebydlil, kteráž v hromady rumu obrácena byla.
29 Iye sadzalemeranso ndipo chuma chake sichidzakhalitsa, ngakhale minda yake sidzabala zipatso pa dziko lapansi.
Avšak nezbohatneť, aniž stane moc jeho, aniž se rozšíří na zemi dokonalost takových.
30 Iyeyo sadzapulumuka mu mdimamo; lawi lamoto lidzawumitsa nthambi zake, ndipo mpweya wochokera mʼkamwa mwa Mulungu udzamusesa.
Nevyjde z temností, mladistvou ratolest jeho usuší plamen, a tak zahyne od ducha úst svých.
31 Asadzinyenge yekha podalira zinthu zachabechabe, pakuti pa mapeto pake sadzaphulapo kanthu.
Ale nevěří, že v marnosti jest ten, jenž bloudí, a že marnost bude směna jeho.
32 Iye adzalandira malipiro ake nthawi yake isanakwane, ndipo nthambi zake sizidzaphukanso.
Před časem svým vyťat bude, a ratolest jeho nebude se zelenati.
33 Iye adzakhala ngati mtengo wamphesa wopululidwa zipatso zake zisanapse, adzakhala ngati mtengo wa olivi umene wayoyola maluwa ake.
Zmaří, jako vinný kmen nezralý hrozen svůj, a svrže květ svůj jako oliva.
34 Pakuti anthu osapembedza Mulungu adzakhala osabala ndipo moto udzapsereza nyumba za onse okonda ziphuphu.
Nebo shromáždění pokrytce spustne, a oheň spálí stany oslepených dary.
35 Iwo amalingalira zaupandu ndipo amachita zoyipa; mtima wawo umakonzekera zachinyengo.”
Kteřížto když počali ssužování, a porodili nepravost, hned břicho jejich strojí jinou lest.

< Yobu 15 >