< Yobu 14 >

1 “Munthu wobadwa mwa amayi amakhala masiku owerengeka ndipo ndi odzaza ndi mavuto okhaokha.
“Nnipa a ɔbea awo wɔn nna yɛ tiaa bi na ɔhaw ahyɛ mu mma.
2 Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota; amathawa ngati mthunzi ndipo sakhalitsa.
Ɔfefɛw te sɛ nhwiren na etwintwam; ɔte sɛ sunsuma a ɛretwa mu akɔ, ɔntena hɔ nkyɛ.
3 Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa? Kodi mungamubweretse pamaso panu kuti mumuzenge mlandu?
Woma wʼani kɔ saa onipa yi so? Wode no bɛba wʼanim abebu no atɛn ana?
4 Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa? Palibe ndi mmodzi yemwe!
Hena na obetumi ayi nea ɛyɛ kronkron afi fi mu? Obiara nni hɔ.
5 Masiku a munthu ndi odziwikiratu; munakhazikitsa chiwerengero cha miyezi yake ndipo munamulembera malire amene sangathe kuwalumpha.
Woahyehyɛ onipa nkwa nna; woahyɛ nʼasram dodow ato hɔ na woahyɛ no bere a ɔrentumi ntra.
6 Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule kufikira atakondwera nawo moyo ngati munthu waganyu.
Enti yi wʼani fi ne so na ɔnyɛ nea ɔpɛ, kosi sɛ obewie nʼadwuma sɛ ɔpaani.
7 “Mtengo uli nacho chiyembekezo: ngati wadulidwa, udzaphukiranso ndipo nthambi zake sizidzaleka kuphukira.
“Dua mpo anidaso wɔ hɔ ma no: Sɛ wotwa a, ɛbɛfefɛw bio, na ne mman foforo no rempenpan.
8 Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka ndipo chitsa chake nʼkuwola pa dothi,
Ne ntin betumi anyin akyɛ asase mu na ne dunsin nso awu wɔ dɔte mu,
9 koma pamene chinyontho chafika udzaphukira ndipo udzaphuka nthambi ngati mtengo wanthete.
nanso, onya nsu a ɛfefɛw, na eyiyi mman sɛ dua a wɔatɛw.
10 Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda, amapuma mpweya wotsiriza ndipo kutha kwake nʼkomweko.
Nanso sɛ nnipa wu a wɔde no hyɛ fam; ɔhome nea etwa to a, na afei onni hɔ bio.
11 Monga madzi amaphwera mʼnyanja kapena monga mtsinje umaphwera nuwuma,
Sɛnea nsu tu yera wɔ po mu no, anaa sɛnea suka mu yowee no,
12 momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso; mpaka zamlengalenga zidzathe, anthu sadzauka kapena kudzutsidwa ku tulo tawo.
saa ara na onipa tɔ fam na ɔnsɔre bio; enkosi sɛ ɔsoro betwa mu no, nnipa rensɔre na wɔrennyan wɔn mfi wɔn nna mu.
13 “Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita! Achikhala munandiyikira nthawi, kuti pambuyo pake mundikumbukirenso. (Sheol h7585)
“Sɛ anka wode me besie ɔda mu de me ahintaw kosi sɛ wʼabufuw betwa mu! Sɛ anka wobɛhyɛ me bere na afei woakae me! (Sheol h7585)
14 Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo? Masiku anga onse a moyo wovutikawu ndidzadikira mpaka itafika nthawi yomasulidwa.
Sɛ onipa wu a ɔbɛba nkwa mu bio ana? Mʼaperedi nna mu nyinaa mɛtwɛn akosi sɛ me foforoyɛ bɛba.
15 Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani; inu mudzafunitsitsa kuona cholengedwa chimene munachipanga ndi manja anu.
Wobɛfrɛ na megye wo so; wʼani begyina abɔde a wo nsa ayɛ.
16 Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga koma simudzalondola tchimo langa.
Afei wobɛkan mʼanammɔntu na worenni me bɔne akyi.
17 Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba; inu mudzaphimba tchimo langa.
Wɔbɛsɔ me bɔne ano wɔ kotoku mu, na woakata mʼamumɔyɛ so.
18 “Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka ndipo monga thanthwe limasunthira kuchoka pa malo ake,
“Nanso sɛnea mmepɔw so hohoro na ɛpompono na ɔbotan nso twe fi ne sibea no,
19 monganso madzi oyenda amaperesera miyala ndipo madzi othamanga amakokololera nthaka, momwemonso Inu mumawononga chiyembekezo cha munthu.
sɛnea nsu yiyi abo ho na osuhweam twe dɔte kɔ no saa ara na wosɛe onipa anidaso.
20 Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu; Inu mumasintha maonekedwe a nkhope yake ndipo mumamutaya kutali.
Wutintim ne so prɛko pɛ, na otwa mu kɔ; wosakra ne nipasu na wugya no kwan.
21 Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo; akamachititsidwa manyazi iye saziona zimenezo.
Sɛ wɔhyɛ ne mmabarima anuonyam a, onnim; na sɛ wɔbrɛ wɔn ase a, onhu.
22 Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake ndipo amangodzilirira yekha mwini wakeyo.”
Ɔno ara were mu yaw na ɔtee na ɔno ara ne ho na ogyam.”

< Yobu 14 >