< Yobu 14 >

1 “Munthu wobadwa mwa amayi amakhala masiku owerengeka ndipo ndi odzaza ndi mavuto okhaokha.
Człowiek, narodzony z niewiasty, dni krótkich jest, i pełen kłopotów;
2 Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota; amathawa ngati mthunzi ndipo sakhalitsa.
Wyrasta jako kwiat, i bywa podcięty, a ucieka jako cień, i nie ostoi się.
3 Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa? Kodi mungamubweretse pamaso panu kuti mumuzenge mlandu?
Wszakże i na takiego otwierasz oczy twoje, a przywodzisz mię do sądu z sobą.
4 Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa? Palibe ndi mmodzi yemwe!
Któż pokaże czystego z nieczystego? Ani jeden;
5 Masiku a munthu ndi odziwikiratu; munakhazikitsa chiwerengero cha miyezi yake ndipo munamulembera malire amene sangathe kuwalumpha.
Gdyż zamierzone są dni jego, liczba miesięcy jego u ciebie; zamierzyłeś mu kres, którego nie może przestąpić.
6 Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule kufikira atakondwera nawo moyo ngati munthu waganyu.
Odstąpże od niego, aż odpocznie, aż przejdzie jako najemniczy dzień jego.
7 “Mtengo uli nacho chiyembekezo: ngati wadulidwa, udzaphukiranso ndipo nthambi zake sizidzaleka kuphukira.
Albowiem i o drzewie jest nadzieja, choć je wytną, że się jeszcze odmłodzi, a latorośl jego nie ustanie.
8 Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka ndipo chitsa chake nʼkuwola pa dothi,
Choć się zstarzeje w ziemi korzeń jego, i w prochu obumrze pień jego:
9 koma pamene chinyontho chafika udzaphukira ndipo udzaphuka nthambi ngati mtengo wanthete.
Wszakże gdy uczuje wilgotność, puści się, i rozpuści gałęzie, jako szczep młody.
10 Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda, amapuma mpweya wotsiriza ndipo kutha kwake nʼkomweko.
Ale człowiek umiera, zemdlony będąc, a umarłszy człowiek gdzież jest?
11 Monga madzi amaphwera mʼnyanja kapena monga mtsinje umaphwera nuwuma,
Jako uchodzą wody z morza, a rzeka opada i wysycha.
12 momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso; mpaka zamlengalenga zidzathe, anthu sadzauka kapena kudzutsidwa ku tulo tawo.
Tak człowiek, gdy się układzie, nie wstanie więcej, a pokąd stoją nieba, nie ocuci się, ani będzie obudzony ze snu swego.
13 “Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita! Achikhala munandiyikira nthawi, kuti pambuyo pake mundikumbukirenso. (Sheol h7585)
Obyżeś mię w grobie ukrył i utaił, ażby się uciszył gniew twój, a iżbyś mi zamierzył kres, kędy chcesz wspomnieć na mię! (Sheol h7585)
14 Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo? Masiku anga onse a moyo wovutikawu ndidzadikira mpaka itafika nthawi yomasulidwa.
Gdy umrze człowiek, izali żyć będzie? Po wszystkie dni wymierzonego czasu mego będę oczekiwał przyszłej odmiany mojej.
15 Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani; inu mudzafunitsitsa kuona cholengedwa chimene munachipanga ndi manja anu.
Zawołasz, a ja tobie odpowiem; a spraw rąk twoich pożądasz.
16 Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga koma simudzalondola tchimo langa.
Aczkolwiekeś teraz kroki moje obliczył, ani odwłóczysz karania za grzech mój.
17 Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba; inu mudzaphimba tchimo langa.
Zapięczętowane jest w wiązance przestępstwo moje, a zgromadzasz nieprawości moje.
18 “Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka ndipo monga thanthwe limasunthira kuchoka pa malo ake,
Prawdziwie jako góra padłszy rozsypuje się, a skała przenosi się z miejsca swego.
19 monganso madzi oyenda amaperesera miyala ndipo madzi othamanga amakokololera nthaka, momwemonso Inu mumawononga chiyembekezo cha munthu.
Jako woda wzdrąża kamienie, a powodzią zalane bywa, co samo od siebie rośnie z prochu ziemi: tak nadzieję ludzką w niwecz obracasz.
20 Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu; Inu mumasintha maonekedwe a nkhope yake ndipo mumamutaya kutali.
Przemagasz go ustawicznie, a on schodzi; odmieniasz postać jego, i wypuszczasz go.
21 Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo; akamachititsidwa manyazi iye saziona zimenezo.
Będąli zacni synowie jego, tego on nie wie; jeźli też wzgardzeni, on nie baczy.
22 Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake ndipo amangodzilirira yekha mwini wakeyo.”
Tylko ciało jego, póki żyw, boleje, a dusza jego w nim kwili.

< Yobu 14 >