< Yobu 14 >
1 “Munthu wobadwa mwa amayi amakhala masiku owerengeka ndipo ndi odzaza ndi mavuto okhaokha.
Et menneske, født av en kvinne, lever en kort tid og mettes med uro.
2 Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota; amathawa ngati mthunzi ndipo sakhalitsa.
Som en blomst skyter han op og visner, han farer bort som skyggen og holder ikke stand.
3 Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa? Kodi mungamubweretse pamaso panu kuti mumuzenge mlandu?
Endog over en sådan holder du dine øine åpne, og mig fører du frem for din domstol!
4 Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa? Palibe ndi mmodzi yemwe!
Kunde det bare komme en ren av en uren! Ikke én!
5 Masiku a munthu ndi odziwikiratu; munakhazikitsa chiwerengero cha miyezi yake ndipo munamulembera malire amene sangathe kuwalumpha.
Når hans dager er fastsatt, hans måneders tall bestemt hos dig, når du har satt ham en grense som han ikke kan overskride,
6 Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule kufikira atakondwera nawo moyo ngati munthu waganyu.
så vend ditt øie bort fra ham, så han kan ha ro så vidt at han kan glede sig som en dagarbeider ved sin dag!
7 “Mtengo uli nacho chiyembekezo: ngati wadulidwa, udzaphukiranso ndipo nthambi zake sizidzaleka kuphukira.
For treet er det håp; om det hugges, så spirer det igjen, og på nye skudd mangler det ikke;
8 Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka ndipo chitsa chake nʼkuwola pa dothi,
om dets rot eldes i jorden, og dets stubb dør ut i mulden,
9 koma pamene chinyontho chafika udzaphukira ndipo udzaphuka nthambi ngati mtengo wanthete.
så setter det allikevel knopper ved eimen av vannet og skyter grener som et nyplantet tre.
10 Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda, amapuma mpweya wotsiriza ndipo kutha kwake nʼkomweko.
Men når en mann dør, så ligger han der, når et menneske opgir ånden, hvor er han da?
11 Monga madzi amaphwera mʼnyanja kapena monga mtsinje umaphwera nuwuma,
Som vannet minker bort i en sjø, og som en elv efterhånden blir grunnere og tørker ut,
12 momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso; mpaka zamlengalenga zidzathe, anthu sadzauka kapena kudzutsidwa ku tulo tawo.
så legger et menneske sig ned og reiser sig ikke igjen; så lenge himmelen er til, våkner de ikke - de vekkes ikke op av sin søvn.
13 “Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita! Achikhala munandiyikira nthawi, kuti pambuyo pake mundikumbukirenso. (Sheol )
Å om du vilde gjemme mig i dødsriket og skjule mig der til din vrede var over - om du vilde sette mig et tidsmål og så komme mig i hu! (Sheol )
14 Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo? Masiku anga onse a moyo wovutikawu ndidzadikira mpaka itafika nthawi yomasulidwa.
Når en mann dør, lever han da op igjen? Alle min krigstjenestes dager skulde jeg da vente, til min avløsning kom;
15 Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani; inu mudzafunitsitsa kuona cholengedwa chimene munachipanga ndi manja anu.
du skulde da rope, og jeg skulde svare dig; efter dine henders verk skulde du lenges.
16 Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga koma simudzalondola tchimo langa.
Men nu teller du mine skritt og akter stadig på min synd.
17 Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba; inu mudzaphimba tchimo langa.
Forseglet i en pung ligger min brøde, og du syr til over min misgjerning.
18 “Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka ndipo monga thanthwe limasunthira kuchoka pa malo ake,
Men som et fjell faller og smuldres bort, og en klippe flyttes fra sitt sted,
19 monganso madzi oyenda amaperesera miyala ndipo madzi othamanga amakokololera nthaka, momwemonso Inu mumawononga chiyembekezo cha munthu.
som vannet huler ut stener og flommen skyller bort mulden, således gjør du menneskets håp til intet;
20 Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu; Inu mumasintha maonekedwe a nkhope yake ndipo mumamutaya kutali.
du overvelder ham for alltid, og han farer bort; du forvender hans åsyn og lar ham fare.
21 Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo; akamachititsidwa manyazi iye saziona zimenezo.
Kommer hans barn til ære, da vet han det ikke, og blir de ringeaktet, da blir han det ikke var.
22 Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake ndipo amangodzilirira yekha mwini wakeyo.”
Bare over ham selv kjenner hans legeme smerte, og bare over ham selv sørger hans sjel.