< Yobu 14 >

1 “Munthu wobadwa mwa amayi amakhala masiku owerengeka ndipo ndi odzaza ndi mavuto okhaokha.
For a mortal born of a woman [is] short lived, and full of wrath.
2 Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota; amathawa ngati mthunzi ndipo sakhalitsa.
Or he falls like a flower that has bloomed; and he departs like a shadow, and can’t continue.
3 Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa? Kodi mungamubweretse pamaso panu kuti mumuzenge mlandu?
Hast you not taken account even of him, and caused him to enter into judgment before you?
4 Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa? Palibe ndi mmodzi yemwe!
For who shall be pure from uncleanness? not even one;
5 Masiku a munthu ndi odziwikiratu; munakhazikitsa chiwerengero cha miyezi yake ndipo munamulembera malire amene sangathe kuwalumpha.
if even his life should be [but] one day upon the earth: and his months are numbered by him: you have appointed [him] for a time, and he shall by no means exceed [it].
6 Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule kufikira atakondwera nawo moyo ngati munthu waganyu.
Depart from him, that he may be quiet, and take pleasure in his life, [though] as a hireling.
7 “Mtengo uli nacho chiyembekezo: ngati wadulidwa, udzaphukiranso ndipo nthambi zake sizidzaleka kuphukira.
For there is hope for a tree, even if it should be cut down, [that] it shall blossom again, and its branch shall not fail.
8 Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka ndipo chitsa chake nʼkuwola pa dothi,
For though its root should grow old in the earth, and its stem die in the rock;
9 koma pamene chinyontho chafika udzaphukira ndipo udzaphuka nthambi ngati mtengo wanthete.
it will blossom from the scent of water, and will produce a crop, as one newly planted.
10 Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda, amapuma mpweya wotsiriza ndipo kutha kwake nʼkomweko.
But a man that has died is utterly gone; and when a mortal has fallen, he is no more.
11 Monga madzi amaphwera mʼnyanja kapena monga mtsinje umaphwera nuwuma,
For the sea wastes in [length of] time, and a river fails and is dried up.
12 momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso; mpaka zamlengalenga zidzathe, anthu sadzauka kapena kudzutsidwa ku tulo tawo.
And man that has lain down [in death] shall certainly not rise again till the heaven be dissolved, and they shall not awake from their sleep.
13 “Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita! Achikhala munandiyikira nthawi, kuti pambuyo pake mundikumbukirenso. (Sheol h7585)
For oh that you had kept me in the grave, and had hidden me until your wrath should cease, and you should set me a time in which you would remember me! (Sheol h7585)
14 Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo? Masiku anga onse a moyo wovutikawu ndidzadikira mpaka itafika nthawi yomasulidwa.
For if a man should die, shall he live [again], having accomplished the days of his life? I will wait till I exist again?
15 Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani; inu mudzafunitsitsa kuona cholengedwa chimene munachipanga ndi manja anu.
Then shall you call, and I will listen to you: but do not you reject the work of your hands.
16 Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga koma simudzalondola tchimo langa.
But you have numbered my devices: and not one of my sins shall escape you?
17 Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba; inu mudzaphimba tchimo langa.
An you have sealed up my transgressions in a bag, and marked if I have been guilty of any transgression unawares.
18 “Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka ndipo monga thanthwe limasunthira kuchoka pa malo ake,
And verily a mountain falling will utterly be destroyed, and a rock shall be worn out of its place.
19 monganso madzi oyenda amaperesera miyala ndipo madzi othamanga amakokololera nthaka, momwemonso Inu mumawononga chiyembekezo cha munthu.
The waters wear the stones, and waters falling headlong [overflow] a heap of the earth: and you destroy the hope of man.
20 Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu; Inu mumasintha maonekedwe a nkhope yake ndipo mumamutaya kutali.
You drive him to an end, and he is gone: you set your face against him, and send him away;
21 Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo; akamachititsidwa manyazi iye saziona zimenezo.
and though his children be multiplied, he knows [it] not; and if they be few, he is not aware.
22 Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake ndipo amangodzilirira yekha mwini wakeyo.”
But his flesh is in pain, and his soul mourns.

< Yobu 14 >