< Yobu 14 >
1 “Munthu wobadwa mwa amayi amakhala masiku owerengeka ndipo ndi odzaza ndi mavuto okhaokha.
As for man, the son of woman, his days are short and full of trouble.
2 Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota; amathawa ngati mthunzi ndipo sakhalitsa.
He comes out like a flower, and is cut down: he goes in flight like a shade, and is never seen again.
3 Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa? Kodi mungamubweretse pamaso panu kuti mumuzenge mlandu?
Is it on such a one as this that your eyes are fixed, with the purpose of judging him?
4 Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa? Palibe ndi mmodzi yemwe!
If only a clean thing might come out of an unclean! But it is not possible.
5 Masiku a munthu ndi odziwikiratu; munakhazikitsa chiwerengero cha miyezi yake ndipo munamulembera malire amene sangathe kuwalumpha.
If his days are ordered, and you have knowledge of the number of his months, having given him a fixed limit past which he may not go;
6 Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule kufikira atakondwera nawo moyo ngati munthu waganyu.
Let your eyes be turned away from him, and take your hand from him, so that he may have pleasure at the end of his day, like a servant working for payment.
7 “Mtengo uli nacho chiyembekezo: ngati wadulidwa, udzaphukiranso ndipo nthambi zake sizidzaleka kuphukira.
For there is hope of a tree; if it is cut down, it will come to life again, and its branches will not come to an end.
8 Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka ndipo chitsa chake nʼkuwola pa dothi,
Though its root may be old in the earth, and its cut-off end may be dead in the dust;
9 koma pamene chinyontho chafika udzaphukira ndipo udzaphuka nthambi ngati mtengo wanthete.
Still, at the smell of water, it will make buds, and put out branches like a young plant.
10 Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda, amapuma mpweya wotsiriza ndipo kutha kwake nʼkomweko.
But man comes to his death and is gone: he gives up his spirit, and where is he?
11 Monga madzi amaphwera mʼnyanja kapena monga mtsinje umaphwera nuwuma,
The waters go from a pool, and a river becomes waste and dry;
12 momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso; mpaka zamlengalenga zidzathe, anthu sadzauka kapena kudzutsidwa ku tulo tawo.
So man goes down to his last resting-place and comes not again: till the heavens come to an end, they will not be awake or come out of their sleep.
13 “Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita! Achikhala munandiyikira nthawi, kuti pambuyo pake mundikumbukirenso. (Sheol )
If only you would keep me safe in the underworld, putting me in a secret place till your wrath is past, giving me a fixed time when I might come to your memory again! (Sheol )
14 Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo? Masiku anga onse a moyo wovutikawu ndidzadikira mpaka itafika nthawi yomasulidwa.
If death takes a man, will he come to life again? All the days of my trouble I would be waiting, till the time came for me to be free.
15 Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani; inu mudzafunitsitsa kuona cholengedwa chimene munachipanga ndi manja anu.
At the sound of your voice I would give an answer, and you would have a desire for the work of your hands.
16 Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga koma simudzalondola tchimo langa.
For now my steps are numbered by you, and my sin is not overlooked.
17 Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba; inu mudzaphimba tchimo langa.
My wrongdoing is corded up in a bag, and my sin is shut up safe.
18 “Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka ndipo monga thanthwe limasunthira kuchoka pa malo ake,
But truly a mountain falling comes to dust, and a rock is moved from its place;
19 monganso madzi oyenda amaperesera miyala ndipo madzi othamanga amakokololera nthaka, momwemonso Inu mumawononga chiyembekezo cha munthu.
The stones are crushed small by the force of the waters; the dust of the earth is washed away by their overflowing: and so you put an end to the hope of man.
20 Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu; Inu mumasintha maonekedwe a nkhope yake ndipo mumamutaya kutali.
You overcome him for ever, and he is gone; his face is changed in death, and you send him away.
21 Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo; akamachititsidwa manyazi iye saziona zimenezo.
His sons come to honour, and he has no knowledge of it; they are made low, but he is not conscious of it.
22 Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake ndipo amangodzilirira yekha mwini wakeyo.”
Only his flesh still has pain, and his soul is sad.