< Yobu 13 >
1 “Ndaziona ndi maso anga zonsezi, ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.
He aquí que todas estas cosas han visto mis ojos, y oído y entendido para sí mis oídos.
2 Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa; ineyo sindine munthu wamba kwa inu.
Como vosotros lo sabéis, lo sé yo: no soy menos que vosotros.
3 Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.
Mas yo hablaría con el Todopoderoso, y querría disputar con Dios.
4 Koma inu mukundipaka mabodza; nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!
Que ciertamente vosotros sois componedores de mentira, todos vosotros sois médicos de nada.
5 Achikhala munangokhala chete nonsenu! Apo mukanachita zanzeru.
Ojalá callando callarais del todo, porque os fuera en lugar de sabiduría.
6 Tsopano imvani kudzikanira kwanga; imvani kudandaula kwa pakamwa panga.
Oíd pues ahora mi disputa, y estád atentos a los argumentos de mis labios.
7 Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu? Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?
¿Habéis de hablar iniquidad por Dios? ¿habéis de hablar por él engaño?
8 Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera? Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?
¿Habéis vosotros de hacerle honra? ¿habéis de pleitear vosotros por Dios?
9 Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa? Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?
¿Sería bueno que él os escudriñase? ¿Burlaros heis con él, como quien se burla con algún hombre?
10 Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani ngati muchita zokondera mseri.
El arguyendo os argüirá duramente, si en lo secreto le hicieseis tal honra.
11 Kodi ulemerero wake sungakuopseni? Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?
Ciertamente su alteza os había de espantar, y su pavor había de caer sobre vosotros.
12 Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo; mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.
Vuestras memorias serán comparadas a la ceniza, y vuestros cuerpos como cuerpos de lodo.
13 “Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule; tsono zimene zindichitikire zichitike.
Escuchádme, y hablaré yo, y véngame después lo que viniere.
14 Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?
¿Por qué quitaré yo mi carne con mis dientes, y pondré mi alma en mi palma?
15 Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira; ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.
Aun cuando me matare, en él esperaré: empero mis caminos defenderé delante de él.
16 Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!
Y él también me será salud, porque no entrará en su presencia el impío.
17 Mvetserani mosamala mawu anga; makutu anu amve zimene ndikunena.
Oíd con atención mi razón, y mi denunciación con vuestros oídos.
18 Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga, ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.
He aquí ahora, que si yo me apercibiere a juicio, yo sé que seré justificado.
19 Kodi alipo wina amene angatsutsane nane? ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.
¿Quién es el que pleiteará conmigo? porque si ahora callase, me moriría.
20 “Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi, ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:
A lo menos dos cosas no hagas conmigo, y entonces no me esconderé de tu rostro.
21 Muchotse dzanja lanu pa ine, ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.
Aparta de mí tu mano, y no me asombre tu terror:
22 Tsono muyitane ndipo ndidzayankha, kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.
Y llama, y yo responderé: o yo hablaré, y respóndeme tú:
23 Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati? Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.
¿Cuántas iniquidades y pecados tengo yo? Házme entender mi prevaricación y mi pecado.
24 Chifukwa chiyani mukundifulatira ndi kundiyesa ine mdani wanu?
¿Por qué escondes tu rostro, y me cuentas por tu enemigo?
25 Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo? Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?
¿A la hoja arrebatada del aire has de quebrantar? ¿y a una arista seca has de perseguir?
26 Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.
¿Por qué escribes contra mí amarguras, y me haces cargo de los pecados de mi mocedad;
27 Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo. Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.
Y pones mis pies en el cepo, y guardas todos mis caminos, imprimiéndolo a las raíces de mis pies?
28 “Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa, ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.
Siendo el hombre como carcoma que se envejece: y como vestido que se come de polilla.