< Yobu 13 >

1 “Ndaziona ndi maso anga zonsezi, ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.
Ятэ, окюл меу а вэзут тоате ачестя, урекя мя а аузит ши а луат сяма.
2 Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa; ineyo sindine munthu wamba kwa inu.
Че штиць вой штиу ши еу, ну сунт май прежос декыт вой.
3 Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.
Дар вряу сэ ворбеск акум Челуй Атотпутерник, вряу сэ-мь апэр причина ынаинтя луй Думнезеу.
4 Koma inu mukundipaka mabodza; nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!
Кэч вой сунтець ниште фэуриторь де минчунь, сунтець ку тоций ниште докторь де нимик.
5 Achikhala munangokhala chete nonsenu! Apo mukanachita zanzeru.
О, де аць фи тэкут, че ынцелепчуне аць фи арэтат!
6 Tsopano imvani kudzikanira kwanga; imvani kudandaula kwa pakamwa panga.
Акум, аскултаць, вэ рог, апэраря мя ши луаць аминте ла рэспунсул бузелор меле!
7 Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu? Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?
Врець сэ ворбиць лукрурь недрепте дин драгосте пентру Думнезеу ши сэ спунець минчунь ка сэ-Л апэраць?
8 Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera? Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?
Врець сэ цинець ку Ел ши сэ фачець пе апэрэторий луй Думнезеу?
9 Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa? Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?
Дакэ вэ ва черчета Ел, ва гэси бине оаре? Сау врець сэ-Л ыншелаць кум ыншелаць пе ун ом?
10 Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani ngati muchita zokondera mseri.
Ну, ну; чи Ел вэ ва осынди дакэ ын аскунс ну лукраць декыт пэртининду-Л пе Ел.
11 Kodi ulemerero wake sungakuopseni? Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?
Ну вэ ынфрикошязэ мэреция Луй? Ши ну каде гроаза Луй песте вой?
12 Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo; mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.
Пэрериле воастре сунт пэрерь де ченушэ, ынтэритуриле воастре сунт ынтэритурь де лут.
13 “Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule; tsono zimene zindichitikire zichitike.
Тэчець, лэсаци-мэ, вряу сэ ворбеск! Ынтымплэ-ми-се че ми с-ар ынтымпла.
14 Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?
Ымь вой луа карня ын динць ши ымь вой пуне вяца ын жок.
15 Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira; ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.
Да, мэ ва учиде: н-ам нимик де нэдэждуит; дар ымь вой апэра пуртаря ын фаца Луй.
16 Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!
Кяр ши лукрул ачеста поате служи ла скэпаря мя, кэч ун нелеӂюит ну ындрэзнеште сэ винэ ынаинтя Луй.
17 Mvetserani mosamala mawu anga; makutu anu amve zimene ndikunena.
Аскултаць, аскултаць кувинтеле меле, луаць аминте ла челе че вой спуне.
18 Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga, ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.
Ятэ-мэ, сунт гата сэ-мь апэр причина, кэч штиу кэ ам дрептате.
19 Kodi alipo wina amene angatsutsane nane? ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.
Аре чинева чева де спус ымпотрива мя? Атунч так ши вряу сэ мор.
20 “Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi, ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:
Нумай доуэ лукрурь фэ-мь ши ну мэ вой аскунде де Фаца Та:
21 Muchotse dzanja lanu pa ine, ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.
Траӂе-Ць мына де пе мине ши ну мэ май тулбура ку гроаза Та.
22 Tsono muyitane ndipo ndidzayankha, kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.
Апой, кямэ-мэ, ши-Ць вой рэспунде сау ласэ-мэ сэ ворбеск еу ши рэспунде-мь Ту!
23 Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati? Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.
Кыте фэрэделеӂь ши пэкате ам фэкут? Аратэ-мь кэлкэриле де леӂе ши пэкателе меле.
24 Chifukwa chiyani mukundifulatira ndi kundiyesa ine mdani wanu?
Пентру че Ыць аскунзь Фаца ши мэ ей дрепт врэжмаш?
25 Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo? Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?
Врей сэ ловешть о фрунзэ суфлатэ де вынт? Врей сэ урмэрешть ун пай ускат?
26 Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.
Пентру че сэ мэ ловешть ку суферинце амаре ши сэ мэ педепсешть пентру грешель дин тинереце?
27 Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo. Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.
Пентру че сэ-мь пуй пичоареле ын бутучь, сэ-мь пындешть тоате мишкэриле, сэ пуй хотар пашилор мей,
28 “Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa, ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.
кынд трупул меу каде ын путрезире, ка о хайнэ мынкатэ де молий?

< Yobu 13 >