< Yobu 13 >

1 “Ndaziona ndi maso anga zonsezi, ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.
Ecce omnia haec vidit oculus meus, et audivit auris mea, et intellexi singula.
2 Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa; ineyo sindine munthu wamba kwa inu.
Secundum scientiam vestram et ego novi: nec inferior vestri sum.
3 Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.
Sed tamen ad Omnipotentem loquar, et disputare cum Deo cupio:
4 Koma inu mukundipaka mabodza; nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!
Prius vos ostendens fabricatores mendacii, et cultores perversorum dogmatum.
5 Achikhala munangokhala chete nonsenu! Apo mukanachita zanzeru.
Atque utinam taceretis, ut putaremini esse sapientes.
6 Tsopano imvani kudzikanira kwanga; imvani kudandaula kwa pakamwa panga.
Audite ergo correptionem meam, et iudicium labiorum meorum attendite.
7 Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu? Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?
Numquid Deus indiget vestro mendacio, ut pro illo loquamini dolos?
8 Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera? Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?
Numquid faciem eius accipitis, et pro Deo iudicare nitimini?
9 Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa? Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?
Aut placebit ei quem celare nihil potest? aut decipietur ut homo, vestris fraudulentiis?
10 Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani ngati muchita zokondera mseri.
Ipse vos arguet, quoniam in abscondito faciem eius accipitis.
11 Kodi ulemerero wake sungakuopseni? Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?
Statim ut se commoverit, turbabit vos, et terror eius irruet super vos.
12 Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo; mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.
Memoria vestra comparabitur cineri, et redigentur in lutum cervices vestrae.
13 “Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule; tsono zimene zindichitikire zichitike.
Tacete paulisper ut loquar quodcumque mihi mens suggesserit.
14 Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?
Quare lacero carnes meas dentibus meis, et animam meam porto in manibus meis?
15 Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira; ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.
Etiam si occiderit me, in ipso sperabo: verumtamen vias meas in conspectu eius arguam.
16 Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!
Et ipse erit salvator meus: non enim veniet in conspectu eius omnis hypocrita.
17 Mvetserani mosamala mawu anga; makutu anu amve zimene ndikunena.
Audite sermonem meum, et aenigmata percipite auribus vestris.
18 Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga, ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.
Si fuero iudicatus, scio quod iustus inveniar.
19 Kodi alipo wina amene angatsutsane nane? ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.
Quis est qui iudicetur mecum? veniat: quare tacens consumor?
20 “Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi, ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:
Duo tantum ne facias mihi, et tunc a facie tua non abscondar:
21 Muchotse dzanja lanu pa ine, ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.
Manum tuam longe fac a me, et formido tua non me terreat.
22 Tsono muyitane ndipo ndidzayankha, kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.
Voca me, et ego respondebo tibi: aut certe loquar, et tu responde mihi.
23 Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati? Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.
Quantas habeo iniquitates et peccata, scelera mea et delicta ostende mihi.
24 Chifukwa chiyani mukundifulatira ndi kundiyesa ine mdani wanu?
Cur faciem tuam abscondis, et arbitraris me inimicum tuum?
25 Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo? Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?
Contra folium, quod vento rapitur, ostendis potentiam tuam, et stipulam siccam persequeris:
26 Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.
Scribis enim contra me amaritudines, et consumere me vis peccatis adolescentiae meae.
27 Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo. Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.
Posuisti in nervo pedem meum, et observasti omnes semitas meas, et vestigia pedum meorum considerasti:
28 “Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa, ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.
Qui quasi putredo consumendus sum, et quasi vestimentum quod comeditur a tinea.

< Yobu 13 >