< Yobu 13 >
1 “Ndaziona ndi maso anga zonsezi, ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.
Lám, mindet látta szemem, hallotta fülem s meg értette.
2 Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa; ineyo sindine munthu wamba kwa inu.
Tudástokhoz képest tudom én is, nem esem messze tőletek.
3 Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.
Azonban én a Mindenhatóval beszélnék s Istennel szemben védekezni kívánok.
4 Koma inu mukundipaka mabodza; nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!
Azonban ti hazugsággal tapasztók vagytok, semmit se gyógyítók mindnyájatok.
5 Achikhala munangokhala chete nonsenu! Apo mukanachita zanzeru.
Vajha hallgatva hallgatnátok, s az bölcseségül lenne nektek!
6 Tsopano imvani kudzikanira kwanga; imvani kudandaula kwa pakamwa panga.
Halljátok csak védekezésemet s ajkaim pörlésére figyeljetek.
7 Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu? Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?
Istenért beszéltek-e jogtalanságot és érte beszéltek csalárdságot?
8 Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera? Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?
Személyét tekintitek-e, avagy Istenért pöröltök?
9 Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa? Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?
Jó lesz-e, midőn kikutat benneteket, avagy mint embert ámítanátok, ámítjátok őt?
10 Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani ngati muchita zokondera mseri.
Feddve fedd majd titeket, ha titokban személyt válogattok.
11 Kodi ulemerero wake sungakuopseni? Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?
Nemde a fensége megrémítene benneteket, s rátok esne rettentése?
12 Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo; mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.
Emlékmondásaitok hamu-példázatok, akár agyag-magaslatok a ti magaslataitok.
13 “Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule; tsono zimene zindichitikire zichitike.
Hallgassatok el előttem, hadd beszélek én, essék meg rajtam bármi is!
14 Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?
Bármiképpen – fogaim között viszem húsomat, s lelkemet tenyeremre teszem.
15 Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira; ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.
Lám, megöl engem: várakozom ő rá; csak útjaimat védeném arcza előtt.
16 Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!
Az is segítségemre való, hogy színe elé nem juthat képmutató.
17 Mvetserani mosamala mawu anga; makutu anu amve zimene ndikunena.
Hallva halljátok szavamat és közlésemet füleitekkel.
18 Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga, ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.
Íme, kérlek, elrendeztem a jogügyet, tudom, hogy nekem lesz igazam.
19 Kodi alipo wina amene angatsutsane nane? ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.
Ki az, ki perbe száll velem, mert most ha hallgatnom kell, kimúlok.
20 “Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi, ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:
Csak kettőt ne tégy velem, akkor színed elől nem rejtőzöm el:
21 Muchotse dzanja lanu pa ine, ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.
Kezedet távolítsd el rólam, és ijesztésed ne rémítsen engem;
22 Tsono muyitane ndipo ndidzayankha, kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.
aztán szólíts és én felelek, vagy beszélek én s te válaszolj nekem.
23 Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati? Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.
Mennyi bűnöm és vétkem van nekem, bűntettemet és vétkemet tudasd velem!
24 Chifukwa chiyani mukundifulatira ndi kundiyesa ine mdani wanu?
Miért rejted el arczodat és ellenségednek tekintesz engem?
25 Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo? Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?
Vajon elhajtott levelet riasztasz-e, és száraz tarlót üldözöl?
26 Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.
Hogy keserűségeket irsz föl ellenem s örökölteted velem ifjúkorom bűneit;
27 Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo. Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.
és karóba tested lábaimat, megvigyázod mind az ösvényeimet, lábaim gyökerei köré húzod jeledet.
28 “Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa, ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.
És ő mint a rothadék szétmállik, mint ruha, melyet moly emésztett: