< Yobu 13 >
1 “Ndaziona ndi maso anga zonsezi, ndazimva ndi makutu anga ndipo ndazimvetsa.
Lo, mine eye hath seen all this, mine ear hath heard and understood it.
2 Zimene inu mukudziwa, inenso ndimazidziwa; ineyo sindine munthu wamba kwa inu.
What ye know, do I know also; I am not inferior unto you.
3 Koma ine ndikulakalaka nditayankhula ndi Wamphamvuzonse ndi kukamba mlandu wanga ndi Mulungu.
Notwithstanding I would speak to the Almighty, and I desire to reason with God.
4 Koma inu mukundipaka mabodza; nonsenu ndinu asingʼanga opanda phindu!
But ye are plasterers of lies, ye are all physicians of no value.
5 Achikhala munangokhala chete nonsenu! Apo mukanachita zanzeru.
Oh that ye would altogether hold your peace! and it would be your wisdom.
6 Tsopano imvani kudzikanira kwanga; imvani kudandaula kwa pakamwa panga.
Hear now my reasoning, and hearken to the pleadings of my lips.
7 Kodi inu mudzayankhula moyipa kuyankhulira Mulungu? Kodi mudzayankhulira Iyeyo mwachinyengo?
Will ye speak unrighteously for God, and talk deceitfully for Him?
8 Kodi mudzaonetsa kuti Iyeyo ngokondera? Kodi inu mudzamuteteza Mulungu pa mlandu wake?
Will ye show Him favour? Will ye contend for God?
9 Mulungu atayangʼanitsitsa, inu nʼkukupezani wosalakwa? Kodi inu mungamunamize Iye monga momwe munganamizire munthu?
Would it be good that He should search you out? Or as one mocketh a man, will ye mock Him?
10 Ndithudi, Iye angathe kukudzudzulani ngati muchita zokondera mseri.
He will surely reprove you, if ye do secretly show favour.
11 Kodi ulemerero wake sungakuopseni? Kodi kuopsa kwake sikungakuchititseni mantha?
Shall not His majesty terrify you, and His dread fall upon you?
12 Mawu anu anzeru ali ngati miyambi yopanda tanthauzo; mawu anu odzitchinjirizira ali ngati mpanda wadothi.
Your memorials shall be like unto ashes, your eminences to eminences of clay.
13 “Khalani chete ndipo ndilekeni ndiyankhule; tsono zimene zindichitikire zichitike.
Hold your peace, let me alone, that I may speak, and let come on me what will.
14 Chifukwa chiyani ndikuyika moyo wanga pa chiswe ndi kutengera mʼmanja moyo wangawu?
Wherefore? I will take my flesh in my teeth, and put my life in my hand.
15 Ngakhale Iye andiphe, komabe ndidzamukhulupirira; ndithu, ndidzafotokoza mlandu wanga pamaso pake.
Though He slay me, yet will I trust in Him; but I will argue my ways before Him.
16 Zoonadi, ichi ndiye chidzakhala chipulumutso changa pakuti palibe munthu wosapembedza amene angafike pamaso pake!
This also shall be my salvation, that a hypocrite cannot come before Him.
17 Mvetserani mosamala mawu anga; makutu anu amve zimene ndikunena.
Hear diligently my speech, and let my declaration be in your ears.
18 Pakuti tsopano ndawukonzekera mlandu wanga, ndikudziwa ndipo adzandipeza wolungama.
Behold now, I have ordered my cause; I know that I shall be justified.
19 Kodi alipo wina amene angatsutsane nane? ngati zili choncho, ndidzakhala chete ndi kufa.
Who is he that will contend with me? For then would I hold my peace and die.
20 “Inu Mulungu, ndipatseni zinthu ziwiri izi, ndipo pamenepo ine sindidzakubisalirani:
Only do not two things unto me, then will I not hide myself from Thee:
21 Muchotse dzanja lanu pa ine, ndipo muleke kundichititsa mantha ndi kuopsa kwanuko.
Withdraw Thy hand far from me; and let not Thy terror make me afraid.
22 Tsono muyitane ndipo ndidzayankha, kapena mulole kuti ine ndiyankhule ndipo Inu muyankhe.
Then call Thou, and I will answer; or let me speak, and answer Thou me.
23 Kodi zolakwa zanga ndi zingati ndipo machimo anga ndi angati? Wonetseni kulakwa kwanga ndi machimo anga.
How many are mine iniquities and sins? Make me to know my transgression and my sin.
24 Chifukwa chiyani mukundifulatira ndi kundiyesa ine mdani wanu?
Wherefore hidest Thou Thy face, and holdest me for Thine enemy?
25 Kodi mudzazunza tsamba lowuluka ndi mphepo? Kodi mudzathamangitsa mungu wowuma?
Wilt Thou harass a driven leaf? And wilt Thou pursue the dry stubble?
26 Pakuti Inu mwalemba zinthu zowawa zonditsutsa nazo ndipo mukundipaka machimo a pa ubwana wanga.
That Thou shouldest write bitter things against me, and make me to inherit the iniquities of my youth.
27 Inu mwamanga miyendo yanga ndi maunyolo. Mumayangʼanitsitsa mayendedwe anga onse poyika zizindikiro pamene mapazi anga apondapo.
Thou puttest my feet also in the stocks, and lookest narrowly unto all my paths; Thou drawest Thee a line about the soles of my feet;
28 “Motero munthu amatha ngati chinthu chofumbwa, ngati chovala chodyedwa ndi njenjete.
Though I am like a wine-skin that consumeth, like a garment that is moth-eaten.