< Yobu 12 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Y respondió Job, y dijo:
2 “Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
Ciertamente que vosotros sois el pueblo, y con vosotros morirá la sabiduría.
3 Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
También tengo yo seso como vosotros: no soy yo menos que vosotros; ¿y quién habrá que no pueda decir otro tanto?
4 “Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
El que invoca a Dios, y él le responde, es burlado de su amigo; y el justo y perfecto es escarnecido.
5 Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
La antorcha es tenida en poco en el pensamiento del próspero: la cual se aparejó contra las caídas de los pies.
6 Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
Las tiendas de los robadores están en paz; y los que provocan a Dios, y los que traen dioses en sus manos, viven seguros.
7 “Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
Mas ciertamente pregunta ahora a las bestias, que ellas te enseñarán; y a las aves de los cielos, que ellas te mostrarán:
8 kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
O habla a la tierra, que ella te enseñará; y los peces de la mar te declararán.
9 Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
¿Qué cosa de todas estas no entiende que la mano de Jehová la hizo,
10 Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
Y que en su mano está el alma de todo viviente, el espíritu de toda carne humana?
11 Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
Ciertamente el oído prueba las palabras, y el paladar gusta las viandas.
12 Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
En los viejos está la ciencia, y en longura de días la inteligencia.
13 “Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
Con el está la sabiduría y la fortaleza, suyo es el consejo y la inteligencia.
14 Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
He aquí, el derribará, y no será edificado: encerrará al hombre, y no habrá quien le abra.
15 Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
He aquí, él detendrá las aguas, y se secarán: él las enviará, y destruirán la tierra.
16 Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
Con él está la fortaleza y la existencia: suyo es el que yerra, y el que hace errar.
17 Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
El hace andar a los consejeros desnudos, y hace enloquecer a los jueces.
18 Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
El suelta la atadura de los tiranos, y les ata la cinta en sus lomos.
19 Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
El lleva despojados a los príncipes, y él trastorna a los valientes.
20 Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
El quita la habla a los que dicen verdad, y el toma el consejo a los ancianos.
21 Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
El derrama menosprecio sobre los príncipes, y enflaquece la fuerza de los esforzados.
22 Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
El descubre las profundidades de las tinieblas, y saca a luz la sombra de muerte.
23 Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
El multiplica las gentes, y él las pierde: él esparce las gentes, y las torna a recoger.
24 Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
El quita el seso de las cabezas del pueblo de la tierra, y los hace que se pierdan vagueando sin camino:
25 Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.
Que palpen las tinieblas, y no la luz: y los hace errar como borrachos.

< Yobu 12 >