< Yobu 12 >
1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Job contestó:
2 “Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
“Ustedes realmente creen que son personas especiales, ¿no es así? Obviamente, cuando mueran, la sabiduría morirá con ustedes.
3 Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
Pero yo también tengo conocimientos, y ustedes no son mejores que yo. ¿No sabe todo el mundo las cosas que han dicho?
4 “Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
Pero mis amigos se ríen de mí porque invoqué a Dios y él me respondió: el hombre inocente que hace el bien se ha convertido en objeto de burla.
5 Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
La gente que está bien desprecia a los que tienen problemas; están dispuestos a empujar a los que ya resbalan.
6 Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
Los ladrones viven en paz, y los que hacen enojar a Dios viven seguros, confiando en su propia fuerza como su ‘dios’.
7 “Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
“Pero si les preguntas a los animales, ellos te enseñarán; las aves del cielo te lo dirán;
8 kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
pregúntale a la tierra y ella te enseñará; y los peces del mar te lo dirán.
9 Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
¿Quién de todos ellos no sabe que el Señor ha hecho esto?
10 Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
Él da vida a todo ser viviente, y a toda la humanidad.
11 Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
El oído distingue palabras como el paladar distingue los alimentos.
12 Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
La sabiduría para distinguir pertenece a los ancianos, y la habilidad para discriminar correctamente pertenece a los que tienen una larga experiencia.
13 “Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
Dios tiene sabiduría y poder, el consejo y el entendimiento le pertenecen.
14 Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
Si derriba algo, nadie puede reconstruirlo. Si encarcela a alguien, nadie podrá liberarlo.
15 Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
Si Dios retiene las aguas, todo se seca; si las suelta, la tierra se inunda.
16 Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
Él es poderoso y victorioso; tanto los engañadores como los engañados están sometidos a él.
17 Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
Lleva a los consejeros despojados de su sabiduría, convierte a los jueces en necios.
18 Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
Él le quita a los reyes sus gruesos collares y los hace vestir taparrabos.
19 Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
Él expulsa a los sacerdotes, despojados de sus vestimentas religiosas, y derriba a los poderosos.
20 Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
Quita el consejo de los consejeros fieles, quita el discernimiento de los ancianos.
21 Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
Derrama el desprecio sobre los príncipes y les quita el poder de los fuertes.
22 Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
Él revela lo que está oculto en las tinieblas, y saca a la luz la sombra de la muerte.
23 Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
Él engrandece a las naciones y las destruye; expande a las naciones y las arruina.
24 Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
Él quita el entendimiento de los gobernantes y los hace vagar por el desierto.
25 Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.
Andan a tientas en la oscuridad, sin luz. Él los hace tambalearse como borrachos”.