< Yobu 12 >

1 Pamenepo Yobu anayankha kuti,
Porém Jó respondeu, dizendo:
2 “Ndithudi inuyo ndinu anthu ndipo nzeru zanu zidzafera nanu pamodzi!
Verdadeiramente vós sois o povo; e convosco morrerá a sabedoria.
3 Koma inenso ndili nazo nzeru ngati inu; ineyo sindine munthu wamba kwa inu. Ndani amene sadziwa zonse zimene mwanenazi?
Também eu tenho entendimento como vós; e não sou inferior a vós; e quem há que não saiba coisas como essas?
4 “Ndasanduka chinthu choseketsa kwa abwenzi anga, ngakhale ndinkapemphera kwa Mulungu ndipo Iye ankandiyankha. Ine ndasanduka chinthu chongoseketsa, ngakhale ndili wolungama ndi wosalakwa!
Eu sou o motivo de riso de meus amigos, eu que invocava a Deus, e ele me respondia; o justo e íntegro serve de riso.
5 Anthu amene ali pabwino amanyoza anzawo amene ali pa tsoka. Tsokalo limagwa pa amene wayamba kale kugwa.
Na opinião de quem está descansado, a desgraça é desprezada, [como se] estivesse preparada aos que cujos pés escorregam.
6 Nyumba za anthu achifwamba zimakhala pa mtendere, ndipo anthu amene amaputa Mulungu amakhala pabwino, amene amanyamula milungu yawo mʼmanja.
As tendas dos ladrões têm descanso, e os que irritam a Deus estão seguros; os que trazem [seu] deus em suas mãos.
7 “Koma funsa nyama zakuthengo ndipo zidzakuphunzitsa, kapena mbalame zamumlengalenga ndipo zidzakuwuza;
Verdadeiramente pergunta agora aos animais, que eles te ensinarão; e às aves dos céus, que elas te explicarão;
8 kapena uyankhule ndi dziko lapansi ndipo lidzakuphunzitsa, kapena ulole nsomba zamʼnyanja kuti zikufotokozere.
Ou fala com a terra, que ela te ensinará; até os peixes do mar te contarão.
9 Kodi mwa zonsezi ndi chiti chimene sichidziwa kuti lachita zimenezi ndi dzanja la Yehova?
Quem entre todas estas coisas não entende que a mão do SENHOR faz isto?
10 Mʼmanja mwake ndi mʼmene muli moyo wa cholengedwa chilichonse, ndiponso moyo wa anthu a mitundu yonse.
Em sua mão está a alma de tudo quanto vive, e o espírito de toda carne humana.
11 Kodi khutu sindiye limene limamva mawu monga mmene lilime limalawira chakudya?
Por acaso o ouvido não distingue as palavras, e o paladar prova as comidas?
12 Kodi nzeru sipezeka pakati pa anthu okalamba? Kodi moyo wautali sumabweretsa nzeru zomvetsa zinthu?
Nos velhos está o conhecimento, e na longa idade o entendimento.
13 “Kwa Mulungu ndiye kuli nzeru ndi mphamvu; uphungu ndi kumvetsa zinthu ndi zake.
Com [Deus] está a sabedoria e a força; o conselho e o entendimento lhe pertencem.
14 Chimene Iye wapasula palibe angachimangenso. Akatsekera munthu mʼndende palibe angamutulutse.
Eis que o que ele derruba não pode ser reconstruído; e ninguém pode libertar o homem a quem ele aprisiona.
15 Iyeyo akamanga mvula dziko limawuma; akamasula mvulayo, madzi amasefukira pa dziko.
Eis que, [quando] ele detém as águas, elas se secam; [quando] ele as deixa sair, elas transtornam a terra.
16 Kwa Iye kuli mphamvu ndi kupambana; munthu wopusitsidwa ndiponso wopusitsa onse ali mu ulamuliro wake.
Com ele está a força e a sabedoria; Seu é o que erra, e o que faz errar.
17 Iye amalanda aphungu nzeru zawo ndipo amapusitsa oweruza.
Ele leva os conselheiros despojados, e faz os juízes enlouquecerem.
18 Iye amachotsa zingwe zimene mafumu anawamanga nazo ndipo amawamanga lamba mʼchiwuno mwawo.
Ele solta a atadura dos reis, e ata um cinto a seus lombos.
19 Iye amasocheretsa ansembe atawalanda nzeru zawo ndipo amagonjetsa anthu amphamvu amene ndi okhazikika.
Ele leva os sacerdotes despojados, e transtorna os poderosos.
20 Iye amakhalitsa chete aphungu odalirika ndipo amalanda chidziwitso cha anthu akuluakulu.
Ele tira a fala daqueles a quem os outros confiam, e tira o juízo dos anciãos.
21 Iye amanyoza anthu otchuka ndipo anthu anyonga amawatha mphamvu.
Ele derrama menosprezo sobre os príncipes, e afrouxa o cinto dos fortes.
22 Iye amatulutsira poyera zinthu zozama za mu mdima ndipo mdima wandiweyaniwo amawusandutsa kuwala.
Ele revela as profundezas das trevas, e traz a sombra de morte à luz.
23 Iye amakuza mitundu ya anthu ndipo amayiwononganso; amachulukitsa mitundu ya anthu ndipo amayimwazanso.
Ele multiplica as nações, e ele as destrói; ele dispersa as nações, e as reúne.
24 Iye amalanda nzeru za atsogoleri a dziko lapansi; amawayendetsa mʼthengo mopanda njira.
Ele tira o entendimento dos líderes do povo da terra, e os faz vaguear pelos desertos, sem caminho.
25 Iwo amafufuzafufuza njira mu mdima wopanda chowunikira; Iye amawayendetsa dzandidzandi ngati oledzera.
Nas trevas andam apalpando, sem terem luz; e os faz cambalear como a bêbados.

< Yobu 12 >